Friday, May 20, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

by Steven Pembamoyo
27/02/2021
in Nkhani
4 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mkokemkoke umene udalipo pakati pa aphunzitsi ndi boma watha tsopano ndipo ophunzira amayenera kubwerera kusukulu dzulo Lachisanu.

Izi zadza kutsatira msonkhano wa atsogoleri a bungwe la aphunzitsi la Teachers Union of Malawi (TUM) ku Lilongwe Lachinayi nduna ya maphunziro Agnes NyaLonje atauza Nyumba ya Malamulo kuti komiti yoona za matenda a Covid 19 idati palibe ndalama za mswahala chifukwa aphunzitsi angakhale pachiopsezo chotenga matenda a Covid 19. M’sabatayi, atsogoleri a TUM adakumana ndi mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera pankhaniyi.

Ndipo Lachinayi masana, wachiwiri kwa wotsatira pulezidenti wa TUM Rehema Harid adati bungwelo lidagwirizana zoti aphunzitsi abwerere kuntchito dzulo Lachisanu.

Iye adati adachita izi potsatira lamulo la Pulezidenti Chakwera kuti aphunzitsi onse ayambe ntchito yawo.

“Ngati bungwe, tikuyenera kutsatira zonena za Pulezidenti ndiye ngati wati tibwerere m’kalasi ife tingakane? Apapa aphunzitsi akubwerera m’kalasi mawa [dzulo],” adatero Harid.

Koma titafunsaso Pulezidenti wawo Willie Malimba adati iye sakugwirizana ndi zomwe adaulutsa achiwiri awowo.

Ophunzira m’sukulu za boma amayenera kuyamba sukulu Lolemba koma izi sizinatheke chifukwa aphunzitsi amanyanyala ntchito zawo pofuna kukakamiza boma kuti liwalipire mswahala wa chiopsezo chotenga matenda a Covid 19 akugwira ntchito.

Sukulu zimayenera kutsegulira Lolembalo mtsogoleri wa dziko lino Chakwera atanena kuti zitero patatha sabata zisanu zili zotsekedwa poopa kufala kwa matenda a Covid 19. Koma pofika Lachinayi maphunziro adali asadayambe.

Ndipo ngakhale Chakwera adakumana ndi bungwe la aphunzitsiwo palibe zidaphula kanthu. Nkhaniyo adaitula ku komiti yoona za matendawa yomwe idati palibe mswahala wotere.

Polankhula m’Nyumba ya Malamulo, nduna ya maphunziro NyaLonje adati komiti yotsogolera polimbana ndi matenda a Covid 19 yati palibe ndalamazo.

Iye adati: “Komitiyo yati aphunzitsi si ali m’gulu la oyenera kulandira mswahala wotere. Pali chitsimikizo choti aphunzitsi adzakhala m’gulu la anthu oyamba kulandira katemera othana ndi matendawa.”

Malimba mmbuyomu adati aphunzitsi adanyanyala ntchito chifukwa boma lidakana limodzi mwa mapempho awo atatu. Iye adati, boma lidavomereza kuonjezera malo ophunzirira ndi kulemba aphunzitsi oonjezera komanso kugula zodzitetezera.

“Sitilowa m’kalasi mpaka nkhani ya mswahara ataivomereza,” adatero Malimba.

Polankhula ndi mtolankhani wathu, kadaulo pa zamaphunziro Benedicto Kondowe adati mpungwepungwewu udadza kaamba ka chidodo cha boma chifukwa aphunzitsiwo adayamba kupempha mswaharawo chaka chatha.

“Koma kusamvana pakati pa TUM ndi boma kwazunzitsa ophunzira. Ena mwa iwo ndi asungwana omwe akutha misinkhu. Iwo amafunika kuthamanga ndi sukulu kuti akamatha msinkhu azikhala atazindikira kufunika kwa sukulu ndiye sakhala ndi maganizo a banja msanga,” adatero Kondowe.

M’masamba a mchezo mukuzungulira kanema wa msungwana wa sukulu ya pulaimale akunena mosapsatira kuti sukulu zikangotsekedwanso basi akupita kubanja.

“Ife asungwana timakula changu kuposa anyamata ndiye izi zoimaima sukuluzi tipezeka kuti takalambira pasukulu. Akangoyerekeza kutsekanso sukulu mwachibwana basi tingopita kubanja,” adatero msungwanayo.

Mlembi wamkulu muunduna wa zamaphunziro Kiswell Dakamau adati boma lalemba aphunzitsi ena 3 270 pofuna kuyankha nkhawa ya aphunzitsi yochepetsa chiwerengero cha ana omwe amayang’aniridwa ndi mphunzitsi mmodzi.

Mneneri kuundunawo Chikondi Chimala adati kupatula kulemba aphunzitsi ena, boma likumanga mabuloko a sukulu 383, lukukumba zitsime 640, kugula mabolodi ophunzitsira ochita kunyamula 5 000 komanso likugula makatoni 13 000 a sopo.

Koma Dakamau adati ngakhale pali zochitika zonsezi, aphunzitsi atemetsabe nkhwangwa pamwala.

“Tayesa kukamba ndi TUM kuti poti zina zonse mwa zofuna zawo zakonzedwa kupatula za mswahara abwerere m’kalasi uku tikukambirana mbali inayo koma ayi akuti sizingatheke,” adatero Dakamau.

Chaka chatha boma lidatsekaso sukulu kwa miyezi 5 ndipo chaka chino zatsekedwa sabata 5 kuchokera pomwe adangotsegulira telemu yoyamba pa 4 January.

Previous Post

Junior Queens yet to start World Cup preparations

Next Post

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post
Trapence: HRDC is bigger than individuals

'Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni'

Opinions and Columns

Business Unpacked

Fixing economy needs action, not rhetoric

May 19, 2022
Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022

Trending Stories

  • CAF accepts FAM’s request on Flames fixture shift

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Onesimus leaves Major One Records

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MCTU pushes for 75% minimum wage hikeof

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Road traffic spot fines on way out

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mayors may face ballots

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.