Sunday, April 11, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Takana kupha makanda

by Bobby Kabango
26/09/2020
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Ife sitivomera kupha makanda.” Uwu ndi uthenga womwe aphungu a Nyumba ya Malamulo auza Tamvani kuti aombera bilo yopatsa mwayi amayi kuchotsa pathupi ikatera m’nyumbayo.

Tamvani m’sabatayi idalankhula ndi aphungu 141 mwa aphungu 188 amene alipo m’dziko muno.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Mimba | The Nation Online
Aphungu akuti bilo yochotsa mimba ayi: Mayi wapakati ku Chileka

Mwa 141, aphungu 113 anenetsa kuti biloyo ikafika m’nyumba ya Malamulo kuti aikambirane, iwo sayerekeza kulola kuti biloyo idutse kukhala lamulo.

Pamene aphungu 26 akuti sadapange chiganizo pa zomwe akachita biloyo ikakafika m’nyumbayo. Aphungu awiri okha ndiwo avomera kuti akalola biloyo kuti idutse.

Aphungu amene akana kuvomera kuti biloyo idutse akuti ndi bwino akapsere zina kumwamba osati chifukwa choti avomereza amayi ndi atsikana kuchotsa pakati.

“Kumenekotu ndi chimodzimodzi kupha kumene. Ineyo monga mkhristu sizoona kuti ndikavotere zimenezo,” adatero Ireen Mambala phungu woima payekha m’boma la Balaka.

Naye Gertrude Nankhumwa ya Blantyre Kabula akuti moyo amapereka ndi Mulungu ndipo Mulungu yekha ndiye ali ndi mphamvu yochotsa.

Susan Ndalama wa ku Blantyre Rural East akuti anthu sadaphunzitsidwe mokwanira zomwe zili mu biloyo komwe kukhale kovuta kuti avomereze.

Phungu wa Mzimba East, Wezzie Gondwe adati ngakhale iye akuvomereza biloyo komabe kukhala kovuta kuti akailole idutse chifukwa anthu a dera lake amakhulupirira kuti kuchotsa pakati ndi tchimo.

Kamlepo Kalua wa ku Rumphi East adati kuvomera biloyo kuli ngati kuwalola anthu kuti atha kumaphana.

“Sindingavomereze biloyo, ndipo sindidzavomerezapo. Kuli ngati kulola kuti tidziphana, ndiye dera langa izi ayi,” adatero Kalua.

Francis Phiso wa kummwera kwa boma la Blantyre komanso Thoko Tembo wa kummwera kwa boma la Neno adati akudikira kaye kuti awerenge bwino biloyo komanso amve maganizo a anthu awo.

Amabungwe ali ndi lingaliro lobweretsa biloyo m’nyumba ya Malamulo pamene aphungu akhale akukumana kuti akaikambirane.

Lingaliro lofuna kubweretsa biloyo lakwiitsa amipingo komanso amabungwe ena amene akupempha aphunguwo kuti asalole kuvomereza kuti biloyo idutsa kusanduka lamulo. n

 Atolankhani awa athandizira, Angela Phiri, Fatsani Gunya, Lucky Mkandawire, Suzgo Chitete ndi Joseph Mwale.

Avatar
Bobby Kabango
Previous Post

On abortion, Parliament jabs

Next Post

UNDP scales up projects to control floods

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
Flood-prone areas to benefit from the project

UNDP scales up projects to control floods

Opinions and Columns

Political Uncensored

Managing the dream

April 11, 2021
My Thought

Malawi needs fixing, not politicking

April 11, 2021
People’s Tribunal

Don’t intimidate Nyasaland Union of Teachers

April 11, 2021
Emily Mkamanga

Longevity in power no solution

April 11, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Malawi Airlines is yet to post a profit since it took to the skies

    Malawi Airlines faces liquidation

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Shareholders, Airtel tussle in court

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MLS wants APM, Muhara property seized

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MHC houses risk demolition

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Industrial disputes choke IRC

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.