Sunday, April 11, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Tambala wameza chimanga

by Bobby Kabango
20/10/2017
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kusadabuzika kwa chipani cha DPP pa chisankho chapadera kukutanthauza kuti Amalawi atopa ndi ulamuliro wa chipanicho, akadaulo a ndale ena atero.

Malinga ndi zotsatira za bungwe loyendetsa chisankho la Malawi Electoral Commission (MEC), pachisankho chapadera chimene chidachitika Lachiwiri m’madera a phungu atatu ndi makhansalanso atatu, chipani cha MCP chidasesa mipando yonse ya phungu ndi iwiri ya khansala pomwe chipani cholamula cha DPP chidapeza mpanda wa khansala umodzi.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

MCP supporters 1 | The Nation Online
Otsatira MCP kusangalala mumzinda wa Blantyre

Akadaulo pankhani za ndale, Henry Chingaipe ndi Mustapha Hussein paokhapaokha adati kusakwaniritsa malonjezo amene DPP idapanga pachisankho cha 2014, ndizo zapangitsa kuti anthu ‘ade nacho kukhosi’.

Hussein adati izi zikutanthauza kuti ‘anthu sakukhutira ndi chipani cholamula cha DPP’ chimene wati sichikukwaniritsa malonjezo ake a pachisankho cha 2014.

“Amalawi sakukhutira ndi momwe [DPP] ikuyendetsera zinthu. Ngati chipanicho sichisintha, adzaona zakuda mu 2019,” adatero Hussein.

Zotsatira za chisankhochi zikudza pamene gulu lofufuza momwe ndale ndi zina zikuyendera mu Africa la Afro-barometer litatulutsa kafukufuku wawo amene amasonyeza kuti ngati chisankho chitachitika lero, Amalawi angavotere MCP pamene amati ataya chikhulupiriro mwa DPP.

Kafukufukuyu atatuluka, chipani cha DPP chidatsutsa ndipo chidati anthu sangayiwale ntchito zabwino zomwe akuchitira Amalawi.

MCP Nsanje Lalanje e1508399929597 | The Nation Online

Hussein wati zotsatira za chisankhochi zikuphera mphongo pa kafukufukuyo. “Vuto chipani cha DPP chimakonda kutsutsa. Koma akuyenera kusinkhasinkha pa zomwe zachitikazi,” adaonjeza.

Naye Chingaipe akuti chisankhochi ndi ‘uthenga kuti anthu atopa ndi ntchito za DPP’. Iye adati chisankhochi chili ngati ‘mpeni wa nsengwa wothwa konsekonse’.

“Mu 2014, DPP idalonjeza zambiri monga kuthana ndi mavuto a kuzimazima kwa magetsi, kusowa kwa madzi, ziphuphu komanso nkhani za umoyo. Mpaka lero palibe chachitika.

“Lero Amalawi apereka uthenga womveka ku boma kuti ngati sasamala, aika chikhulupiriro chawo pa chipani cha MCP,” adatero Chingaipe.

Koma mneneri wa boma Nicholas Dausi adati avomereza kuti agonja. “Ayi tivomere, tagonja ndewu koma nkhondo sitidagonje,” adatero Dausi.

Iye adati abwerera kwa Amalawi kuti amve pakhota nyani mchira kuti mpaka ziwavute choncho.

Wachiwiri kwa mlembi wa MCP Eisenhower Mkaka wati ichi ndi chizindikiro kuti chipanichi chidaberedwa mavoti mu chisankho cha 2014.

“Mwaona nokha zotsatira, tanthauzo kuti mu 2014 adatibera mavoti. Tili ndi chiyembekezo kuti mu 2019 chipani chathu chidzapambana,” adatero Mkaka.

Polengeza Mkulu wa bungwe loyendetsa chisankho la MEC, Jane Ansah Lachitatu adalengetsa zotsatira za chisankho chapadera chomwe chidachitika m’madera atatu.

Chipani cha MCP chidapeza mipando ya kumpoto kwa  Lilongwe Msozi, komwe adapambana ndi Sosten Gwengwe; kumwera cha kummawa kwa mzinda wa Lilongwe kumene adatola chikwama ndi Ulemu Msungama pomwe Lawrence Sitolo adatenga mpando wa ku Nsanje Lalanje.

Ndipo chipanicho chidazomolanso mipando ya khansala wa kuwodi ya  Mtsiriza ku Lilongwe komwe adapambana ndi Kingwell Zikaola komanso kuwodi ya Ndirande Makata kumene adapambana ndi Thom Litchowa.

Wopambana yekhayo wa DPP adali Nicholas Josiya yemwe adatenga wodi ya kumpoto kwa Mayani ku Dedza.

Avatar
Bobby Kabango
Previous Post

Season of jacarandas

Next Post

Egenco, Escom should revisit 2012-2014 strategy

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post

Egenco, Escom should revisit 2012-2014 strategy

Opinions and Columns

Political Uncensored

Managing the dream

April 11, 2021
My Thought

Malawi needs fixing, not politicking

April 11, 2021
People’s Tribunal

Don’t intimidate Nyasaland Union of Teachers

April 11, 2021
Emily Mkamanga

Longevity in power no solution

April 11, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Malawi Airlines is yet to post a profit since it took to the skies

    Malawi Airlines faces liquidation

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MHC houses risk demolition

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Shareholders, Airtel tussle in court

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MLS wants APM, Muhara property seized

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • IMF cancels K9bn debt

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.