Friday, May 20, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Tame Mwawa: Chiphwanya wa Tikuferanji

by Steven Pembamoyo
23/05/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Sewero la Tikuferanji ndi limodzi mwa masewero omwe amapereka phunziro kwa anthu pazochitika mmoyo wa tsiku ndi tsiku komanso ndi msangulutso kwa anthu ambiri. Seweroli limaonetsedwa pakanema komanso kumveka pawailesi ya MBC. Tidachita chidwi ndi mmodzi mwa omwe amachita nawo seweroli, Tame Mwawa, yemwe ambiri amamudziwa kuti Chiphwanya museweromo ndipo ndidacheza naye motere:

Chiphwanya: Mnyamata wazikhakhali pa Tikuferanji
Chiphwanya: Mnyamata wazikhakhali pa Tikuferanji

Ndikudziwe mnzanga.
Ndine Tame Mwawa ndipo ndimakhala ku Machinjiri ku Blantyre koma kwathu ndi ku Chiradzulu, m’mudzi mwa Kambalame, T/A Mpama.

Udabadwa liti?
Ndidabadwa pa 26 October, 1977 ndipo ndine woyamba m’banja la ana 7, amuna 5 ndi asungwana awiri.

Mbiri yako pazisudzo njotani?
Ndikhoza kunena kuti ndidabadwa wazisudzo kale. Abale anga amandiuza kuti ndili wamng’ono ndikadziongola kapena ndikamalira anthu amandiunjirira nkumaseka ndipo makolo anga adadziwiratu kuti ndidzakhala msangalatsi. Kusukulu anzanga ngakhalenso aphunzitsi ankachita kudziwa kuti Tame wabwera zilango ndiye zidali zosatha. Nthawi zina ndinkalembedwa pa anthu olongolola koma pomwe sindidapite kusukulu nkomwe. Pachikondwerero chokumbukira ufulu wa dziko ndinkapanga nawo zisudzo ndipo malipiro ake adali Fanta ndi mpunga wa nyama. Ndinkapanganso sewero la Ambuye Yesu.

Udapezeka bwanji musewero la Tikuferanji?
Nthawi ina yake ankakajambula seweroli pafupi ndi kwathu ndiye penapake pamafunika sing’anga koma munthu amasowa tsono ine ndidadzipereka kuti ndiyesere ndipo ndidachita bwino basi kulowa m’seweroli kudali komweko. Panthawi imeneyo ndidadziwana ndi akuluakulu ena a zisudzo monga Frank Yalu (Nginde) yemwe adanditenga kukalowa gulu lake la zisudzo lotchedwa Kasupe Arts Theatre. Pano ndidadziwika kwambiri moti ndimapezeka m’magulu a zisudzo osiyanasiyana monga Kwathu komanso mumafilimi osiyanasiyana. Imodzi mwa mafilimu omwe ndilimo ndi ya Ching’aning’ani yomwe ikuoneka pakanema ya Malawi komanso ndidayambitsa nawo pologalamu ya Phwete pakanema yemweyu. Pawailesi ndimapanga nawo Sewero la Sabata Ino.

Dzina la Chiphwanya lidayamba bwanji?
Kumudzi kwathu ku Chiradzulu kuli mkulu wina dzina lake Chiphwanya yemwe ndi wolongolola komanso wosachedwa kupsa mtima ndiye nditaona malo omwe ndimapatsidwa m’masewero ambiri ndidaona kuti dzinali ndilondiyenera.

N’zoona kuti pakhomo pako udadzala zikho zambiri?
Eya, ndimadziwiratu mbali zomwe anzanga amakonda kundipatsa pazisudzo motero ndidadzala zikho zambiri komanso mikanda pakhomo panga ili mbweee, moti anthu ena amaona ngati ndimapangadi zausing’anga.

Nanga mano adaguluka n’chiyani?
Munthune ndimavutika ndi mutu kwambiri moti umati ukandimenya mano angapo amayenera kuchoka basi. Bambo anganso n’chimodzimodzi moti iwo mano awo ammwamba adatha onse. Komabe ndimathokoza Mulungu kuti mutuwo sindimadwaladwala.

Uli ndi gulu la zisudzo lakolako?
Ayi, pakadalipano ndilibe, ndimagwira ndi magulu ena ndi mabungwe. Ndimaopa kuthamangira kutero chifukwa ndimaona zokhoma zomwe anzanga ena omwe ali ndi magulu amakumana nazo ngakhale kuti masomphenya otero alipo.

Tags: AdraHIV AidsMichael UsiTikuferanji
Previous Post

Akufuna mwana

Next Post

Gerald Phiri nets in Flames’ loss

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post
Opened the scoresheet:: Phiri Jnr

Gerald Phiri nets in Flames’ loss

Opinions and Columns

Business Unpacked

Fixing economy needs action, not rhetoric

May 19, 2022
Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022

Trending Stories

  • CAF accepts FAM’s request on Flames fixture shift

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Onesimus leaves Major One Records

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MCTU pushes for 75% minimum wage hikeof

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Road traffic spot fines on way out

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mayors may face ballots

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.