Tuesday, May 24, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Thirani manyowa mwachangu

by Nation Online
19/09/2020
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Woona za kafukufuku wa za nthaka ku nthambi ya zakafukufuku wa zaulimi ya Bvumbwe m’boma la Thyolo Peter Mfune akuti kuthira manyowa mwachangu m’munda n’kopindulitsa.

Iye adati kuthira manyowa mwachangu kumathandiza kuti alowerere bwino m’nthaka choncho mlimi akabzala mbewu pomera imapezana ndi chakudya chokwanira ndipo imakula mwa mphamvu ndi kubereka bwino.

Mfune adaonjeza kuti m’zaka zina mvula yoyambirira imatsogozana ndi ng’amba kotero mlimi akathira manyowa moyambirira dothi limakwanitsa kusunga chinyontho kwa nthawi yaitali.

“Zotsatira zake mbewuzo zimapirira kung’amba ndipo sizipserera,” adafotokoza motero.

Alimi ayenera kukonza manyowa msanga, mvula isanadze

Malingana ndi katswiri wa zaulimi wa mbewu ku Lilongwe University of Agriculture and Natural Resources (Luanar) Vernon Kabambe, mbewu za m’munda mmene mwathiridwa manyowa zimakhala kwa sabata ziwiri osaonongeka kukachita ng’amba.

“Manyowa amasunga chinyontho komanso mbewu zimene zalimidwa pa dothi la manyowa zimakhala za mphamvu ndipo zimakula mwachangu,” adatero iye.

Kuonjezera pa izi, mlangizi wa mbewu wa m’chigawo cha zaulimikwaLobim’boma la Dedza adaonjeza kuti kuthira manyowa nthawi yabwino kumathandiza kupewa kuchulukitsa ntchito pamene mvula yagwa.

Iye adati kuthira manyowa ndi ntchito yaikulu chifukwa amafunika ochuluka kuti akwanire munda wonse choncho mlimi akachedwa zotsatira zake amangothira chigawo chochepa kwinako n’kusiya.

“Mvula ikagwa zochitika kumunda zimachuluka zotsatira zake kuthira manyowa kumasiyidwa kaye m’mbuyo choncho popewa izi ndi bwino kuthiriratu.

“Kwa alimi amene amathirabe manyowa osapsa kuthira mochedwa kumaika pachiopsezo mbewu zawo chifukwa amakaotcha mbewu zija,” adatero mlangiziyo.

Chifukwa choti Eneles Timothy wa ku Ntonda m’boma la Blantyre amadaliramanyowa pa ulimi wake, amayesetsa kukonza ndi kuthira manyowa m’munda mwake mwachangu.

Iye adati amatsatira bwino ulangizi wa manyowa kutengera ndi mmene adaphunzitsiridwa choncho amapindula nawo.

“Ndi zoonadi kukachita ng’amba mbewu zanga sizifota msanga.

“Ndimakwanitsa kukonza ndi kuthira manyowa m’munda wanga onse ndisanafike mwezi wa October choncho mvula yobzalira ikagwa sindipanikizika ndimangoona zobzala basi,” adafotokoza motero.

Malingana ndi Mfune, kathiridwe ka manyowa m’munda kamatengera kuchuluka kwa manyowa amene mlimi ali nawo.

Iye adafotokoza kuti ngati mlimi ali ndi manyowa ochuluka, azithira manyowa mu khwawa lonse kapena kuti pakati pa mizere iwiri ndipo awakwirire akamapanga mizere yatsopano yobzalamo mbewu m’chaka chimenecho.

Ngati manyowa ndi ochepa, iye adati mlimi ayambe wapanga mizere m’munda mwake ndi kukumba mapando obzalamo mbewu pamlingo woyenera ndipo akatero athire manyowa m’mapandomo.

“Mvula ikagwa mlimiyo amayenera adzabzale mbewu m’mapando momwe adathira manyowa,” adatero iye.

Mfune adaonjeza kuti kuchuluka kwa manyowa amene mlimi akuyenera kuthira m’munda kumatengera michere imene ili kale m’nthakamo choncho alimi amayenera kuyezetsa nthaka yawo.

Ngakhale izi zili chomwechi, iye adati matani a manyowa osachepera 2.5 amafunika kuthira pa hekitala imodzi. 

Previous Post

FAM hunting for friendlies

Next Post

Akupha makwacha ndi kuchulukitsa mbuzi za chi ‘boer’

Related Posts

Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

May 22, 2022
Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
Next Post
Ulimi wa mbuzi ndi wophweka poyerekeza ndi wa ziweto zina

Akupha makwacha ndi kuchulukitsa mbuzi za chi ‘boer’

Opinions and Columns

People’s Tribunal

What was that press briefing all about?

May 22, 2022
Big Man Wamkulu

Wife, in-law plotting my downfall

May 22, 2022
My Thought

Tonse Alliance died on arrival

May 22, 2022
Layman's Reflection

New IMF programme pivotal moment for Tonse Alliance

May 21, 2022

Trending Stories

  • Musician Martse in hospital after fire accident

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Kalindo earmarked for diplomatic post

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Witness U-turns in Batatawala, 3 others case

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi overlooks players diet

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • How loans get wasted

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.