Saturday, May 21, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Tidakumana ku BICC

by Martha Chirambo
29/11/2020
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Themba William Mwale  adamuona koyamba  Grace Kadzakumanja  kumalo a zochitikachitika a Bingu International Convention Centre (BICC) komwe onse ankakatola nkhani.

Kadzakumanja adapita kumalowa ngati wokajambula zithunzi za kanema wa Channel for All Nations (CfAN) komwe amagwira ntchito, pamene Mwale adapita ngati mtolankhani kuchokera kunyumba youlutsa mawu ya Voice of Livingstonia, ofesi yawo ya ku Lilongwe.

“Ngakhale sitinayankhulane, chithunzithunzi chake chidakhazikika m’malingaliro anga, ndipo ndidamva kuchokera pansi pamtima wanga kuti uyu ndiye wanga wolonjezedwa uja,” adatero Mwale.

Ngakhale awiriwo amakhala mumzinda umodzi wa Lilongwe, zidatenga pafupifupi miyezi iwiri kuti aonanenso. Adaonananso kuhotelo ya Crossroads kogwira ntchito.

Mwale ndi Kadzakumanja lero ndi banja

Panthawi ya chisankho chapatatu cha 2019, Mwale adali ndi atolankhani anzake amuna pamalo ena oponyera voti mumzinda wa Lilongwe pomwe anyamatawa ankalankhula zambiri zotama Kadzakumanja m’maonekedwe angakhalenso khalidwe.

“Apa mpomwe ndinazindikira kuti ndikapitiriza kuchita chidodo, ndidzalilira ku utsi. Apa mpomwe ndinapanga chisankho choti ndiyambe kufunafuna nambala yake kwa anzake ogwira naye ntchito,” iye adatero.

Mwamwayi mmodzi wa ogwira  ntchito ndi Kadzakumanja yemwenso adali mnzake wa Mwale, adamukomera mtima ndikumupatsa nambalayo.

 Apa mpomwe adayamba kucheza momasuka, mpaka kufunsirana ndipo awiriwo anakwatirana pa 3 October 2020 ku Mzimba CCAP pomwe madyelero ake adali ku Mame Motel ku Mzimbako.

Pakadalipano, Mwale ndi  mkulu wa wailesi ya Voice of Livingstonia (VoL) pamene Kadzakumanja ndi mtolankhani ku CfAN, koma akupitiriza kaye maphunziro ake a ukachenjede pa sukulu ya Mzuzu University komwe akupanga maphunziro a Communication Studies.

Mwale amachokera m’mudzi mwa Chibisa kwa Jenda, Mfumu Mabilabo m’boma la Mzimba ndipo Kadzakumanja amachokera m’mudzi mwa Njolomole, Mfumu Njolomole m’boma la Ntcheu.

Previous Post

Nkhanza zanyanya

Next Post

Anatchereza

Related Posts

Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Next Post

Anatchereza

Opinions and Columns

Layman's Reflection

New IMF programme pivotal moment for Tonse Alliance

May 21, 2022
Family Table Talk

Historical lessons on the value of forgetting

May 21, 2022
My Diary

Politics of ‘kutola chikwama’

May 21, 2022
Bottom Up

Ukraine war: Sanctions backfire?

May 21, 2022

Trending Stories

  • Left economy in tatters: Muluzi

    Malawi’s public debt now at K5.8 tn

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • CAF accepts FAM’s request on Flames fixture shift

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Onesimus leaves Major One Records

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Gaba comes up with two options

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • UN bets K66bn on LMC’s plan

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.