Sunday, May 29, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

‘Tidasala masiku 52 kuti Mulungu atiunikire’

by Steven Pembamoyo
25/12/2016
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Nthawi zambiri, anthu timatenga banja ngati sitepe pamoyo wathu basi koma tikalingalira momwe banja la m’busa komanso mlembi wa mkulu wa mpingo wa CCAP Reverend Vasco Kachipapa Banda ndi mkazi wake Madalitso Nyoli, mibadwo yobwerayi idzazindikira momwe banja la umulungu limakhalira.

Awiriwa akuti adakumana mu 1992 onse atasankhidwa kupita kusukulu ya sekondale ya Mitundu ndipo chikondi chawo chidayamba mu 1994 koma uku sikudali kuyamba kwa banja poti zambiri zidadutsapo.

Rev. Kachipapa adati mizati itatu ndiyo idagwira ntchito kuti awiriwa atseguke mmaso kutidi adalengedwa kudzakhala limodzi ndi kutumikira Chauta ngati bambo ndi mayi komanso odyetsa ndikusamala nkhosa zake.

Kachipapa ndi Madalitso: Lero ndi banja

“Mzati woyamba, ineyo ndidadwala tikadali kusukulu mpaka ndidapita kunyumba. Nditapeza bwino nkubwerako, Madalitso adabwera kudzandizonda ndipo aka sikadali komaliza. Pamenepa ndidazindikira kuti ndi umunthu weniweni,” adatero Kachipapa.

Iye adati chikondichi sichidasanduke mapeto azonse ayi koma chiyambi cha kudzifunsa ndi kupempha utsogoleri wa Mulungu.

“Mchaka cha 1997, tonse awiri tidayamba mapemphero ndi kusala kwa masiku 52 (Loweruka lokhalokha) kupempha Mulungu kuti atiunikire ngatidi tidali oyenera kukwatirana. Ndi mzati wachiwiri ndipo mzati wachitatu udali nthawi yomwe ine ndimapanga maphunziro a zaubusa ku Zomba, mkazi wanga adali atayamba kale ntchito ndipo adandithandiza kupereka malowolo ake omwe,” adatero Kachipapa.

Iye adati Chauta atavomereza zonse, ndondomeko zoyenera zidatsatidwa kufikira nthawi ya chinkhoswe m’chaka cha 1998 ndipo kenako ukwati woyera ku Ntchisi CCAP.

“Ndimakonda mkazi wanga kwambiri chifukwa cha mtima wake wabwino, amakonda kupemphera kwambiri ndipo simkazi wanga chabe koma mzanga muuzimu,” adatero Kachipapa.

Nawo mayi a kunyumba akuti (Madalitso) akuti abusawa ndi bambo wabwino wokonda banja lawo ndi wodziwa kusamala.

“Ndi bambo abwino kwambiri odziwa udindo wawo ndiokonda banja lawo komanso kusamala ana awo. Timapemphera limodzi, kuyenda limodzi, kudya limodzi mwachidule timapangira zinthu limodzi,” adatero mayiwo.

Kachipapa amachokera m’mudzi wa Makwenda mfumu yaikulu Chiseka ndipo Madalitso amachokera m’mudzi wa Khanda T/A Kalolo onse m’boma la Lilongwe. n

Previous Post

Khirisimasi ya Niko

Next Post

Party manifesto: Not agenda for the country

Related Posts

Nkhani

Woimba abedwa mumzinda wa mzuzu

May 28, 2022
Nyumba ndi katundu zambiri zidawonongeka ndi Anna komanso Gombe
Nkhani

K34.8 biliyoni ya ngozi zadzidzidzi

May 28, 2022
Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

May 22, 2022
Next Post

Party manifesto: Not agenda for the country

Opinions and Columns

Off the Shelf

Poor timing of Aggreko decommissioning now hurting

May 28, 2022
My Diary

Corruption as an elephant

May 28, 2022
Business Unpacked

Tame egos, take risks to grow economy

May 26, 2022
People’s Tribunal

What was that press briefing all about?

May 22, 2022

Trending Stories

  • People travel on the first part of the East Bank road from Thabwa

    K14bn road fund down the drain

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • ACB sleeps on Bingu’s wealth investigation

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Acb explains Sattar miss

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • RBM justifies devaluation stance

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Bullets , Silver Strikers renew rivarly

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.