Thursday, February 25, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Tikolole motani chimanga?

by ESMIE KOMWA
23/03/2019
in Chichewa
4 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Alimi m’madera a dziko lino amakolola chimanga mosiyanasiyana malingana ndi kuzolowera kwawo koma mphunzitsi wa kunthambi ya za maphunziro a za ulangizi ku Lilongwe University of Agriculture and Natural Resources (Luanar) Paul Fatch akuti njirazi zili ndi ubwino ndi kuipa kwake. Chachikulu, iye adati mlimi amayenera kukonzekera kuthana ndi zinthu zomwe zikhoza kudza kaamba ka njira yomwe akugwiritsa ntchito. ESMIE KOMWA adacheza naye motere:

maize 3 | The Nation Online
Alimi ena amayamba atsenga ndikuika m’mikuku

Kodi ndi zinthu zanji zomwe mlimi akuyenera kukonzekera pokolola chimanga?

RelatedHeadlines

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

Aphungu akumana lolemba

Ndi ana omwe akudzipha

Mlimi ayenera akonzekera masaka kapena malona oikapo chimanga akamakolola kuti chisakhudze pansi, zonyamulira chimanga chake akamaliza kukolola komanso kukonza pofikira mbewuyi kunyumba. Chinthu china chomwe akuyenera kukumbukira n’choti nankafumbwe sachedwa kulowa m’chimanga ndi kuyamba kuononga choncho akuyenera kukonzekera kutonola ndi kuthira mankhwala mwachangu. Chifukwa cha ichi, mlimi aganizire za matumba, mankhwala ophera anamkafumbwe ndi malo osunga kuti akamaliza kukolola, chisakhalitse chisadaikidwe mankhwala.

Nanga ndi zizindikiro zanji zosonyeza kuti chimanga chafika pokololedwa?

Mlimi amayenera akolole chimanga chake pamene chaloza pansi. Panthawiyi, chimanga chimakhala chakhwima komanso chauma bwino choncho kuchisunga sichionongeka.

Kodi mlimi amayenera akolole chimanga chake motani?

Pali njira ziwiri zokololera chimanga. Njira yoyamba ndi yoika m’mikuku kapena kuti m’milu. Njirayi, choyambirira mlimi amadula mapesi chimanga chenichenicho chidakali kumapesiwo n’kumachiunjirira pamodzi. Akamaliza kudulako, amadikira kwa masiku angapo kenako amayamba kuchotsa chimanga ku mapesiwo. Njira yachiwiri, ndi yongokochola chimanga osati kuika m’mikuku. Njirayi, mlimi amangolowa m’munda n’kuyamba kusenda chimanga paphesi lililonse mpaka kumaliza munda onse.

Ubwino wa njira yoika m’mikuku ndi wotani?

Ubwino woyamba ndi woti chimanga chimamalizika kuuma bwino chikakhala pamkukupo kwa masiku angapo. Ubwino wina ndi woti zimathandizira kuti mlimi athe kuchotsa chimanga chonse m’mundamo chifukwa koyambirira amakhala ngati wasetsa mapesi onse a chimanga n’kuwaika pamodzi komanso posenda, amatenga phesi limodzi kufikira amalize. Chimanga amachiika paokha mapesi paokha.

Nanga kuipa kwa njirayi  n’kotani?

Mwatsoka, ngati kwagwa mvula chimanga chija chidakali pamkuku, chimanyowa kotero china chimaonongeka. Chimanga chikakhalitsa pamkukupo, chimakweredwa ndi chiswe. Kuipa kwina n’koti n’kovuta kuchita ulimi wa mleranthaka chifukwa mlimi amakhala ngati wachotsa mapesiwo.

Nanga ubwino wochithyola ndi wotani?

Njirayi ndi yabwino kumbali ya ulimi wa mleranthaka chifukwa pakapita nthawi, mlimi ngati akutsatira ulimiwu, amayenera adule mapesi aja n’kuwagoneka pansi kuti aolerane.

Nanga kuipa kwa njirayi n’kotani?

Chimanga ngati chakololedwa chisanaumitsitse, mlimi amayenera akakafika nacho kunyumba akayanike kufikira chitauma bwino. Kuipa kwina n’koti, kumafuna kuonetsetsa pokolola paja chifukwa kupanda kutero, chimanga china chimatsalira m’munda momwemo.

Nanga ndi zinthu zanji zomwe mlimi akuyenera kusamalitsa pokolola?

Choyambirira, akamachotsa chimanga chija ku mapesi ndikumaika pamulu asamaponye chifukwa china chimasorekera m’munda momwemo. Ndi bwino kuti pamulu pomwe akuikapo chimanga chosendasenda, aziyalapo chinthu kuti ngati china chizisoleka, chizigwerapo ndipo athe kuchitengera kunyumba komanso zimathandizira kuti chisagunde pansi pomwe pakhoza kukhala chinyontho. Chinthu china, mlimi akamaliza kukolola munda wonse, akuyenera ayendere kuonetsetsa kuti chimanga chonse wachotsa m’mundamo.

Nanga mawu anu omaliza kwa alimi pamene akukonzekera kukolola chimanga ndiotani?

Chinthu china chofunikira kwambiri ndi choti alimi apewe zitsotso ku mbewuyi pamene akukolola chifukwa zimayambitsa chukwu. Chukwu ndi choopsa chifukwa chimatulutsa poyizoni yemwe amachepetsa chitetezo cha m’thupi choncho munthu amadwaladwala kapena kumwalira kumene. Kuonjezera apo, chimayambitsa matenda a khansa, chimasokoneza mphamvu yobereka, chimachepetsa chilakolako cha chakudya komanso chimaononga malonda a chimanga.

Previous Post

Government keen to improve business environment

Next Post

Economy under siege

Related Posts

Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Parliament in session
Nkhani

Aphungu akumana lolemba

February 19, 2021
An illustration of court proceedings
Chichewa

Ndi ana omwe akudzipha

February 14, 2021
Next Post
graph 4 | The Nation Online

Economy under siege

Opinions and Columns

My Thought

Malawi needs fixing, not politicking

February 21, 2021
Political Uncensored

No longer at ease..

February 21, 2021
Emily Mkamanga

Discipline paramount in government

February 21, 2021
People’s Tribunal

Let OPC be standard for everyone to follow

February 21, 2021

Trending Stories

  • Co-chaired the task force: Phuka (L) and Mwanamvekha

    K780M Dodma Covid-19 feast

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Bushiri’s daughters blocked from flying out

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Censorship Board acts on ‘Aunt Nellie’ videos

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Convention In July 2023—DPP

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mathanga, kunje Sue president, MEC

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.