Tuesday, April 20, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Woyendetsa ambulansi ataledzera amangidwa

by Martha Chirambo
22/03/2020
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Dalaivala wa ambulansi ya pachipatala cha boma cha Chiradzulu zake zada atagwetsa galimotoyo m’ngalande chifukwa choledzera.

Malinga ndi kanema imene yakhala ikuzungulira m’masamba a mchezo, dalaivalayo akuoneka ali thapsa ndi mowa, akukanika kulankhula zomveka komanso kuima bwinobwino.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

dalaiva | The Nation Online
Ali ku Chichiri: Thumba

Padakalipano mkuluyo ali pa alimande kundende ya Chichiri ndipo akaonekera kubwalo la milandu Lolemba.

Pakanemapo mkuluyo adachita anthu ena adachita kumugwira uku ndi uko. Anthuwo sadamusiye ngakhale amachita makani n’kumakana kuti asamujambule, apatu nkuti galimotoyo italowa m’ngalande mbali mwa msewu wochokera ku Njuli kupita ku Chiradzulu.

Galimotolo ndi gulu la galimoto zatsopano zomwe boma lapereka m’zipatala. Koma mwatsoka, m’galimotomo adanyamulamo wodwala amene amapita naye pachipatalapo.

Andrew Thumba wa zaka 37, yemwe amayendetsa MG 566 AM adathera m’manja mwa anthu omwe adamugwira ndi kuiperanso nkhaniyo kwa akuluakulu a boma.

Ndipo mneneri wa polisi m’bomali Yohane Tasowana watsimikiza za nkhaniyi.

Iye adati mkuluyu akuyankha mlandu woyendetsa galimoto ataledzera mosemphana ndi gawo 128 la malamulo oona za pamsewu m’dziko muno.

Tasowana adatsimikizanso kuti m’galimotomo mudali wodwala yemwe adangonyamulidwa pa njinga ndi anthu achifundo kuthamangira naye kuchipatalako.

Koma mkulu woona za umoyo m’boma la pankhaniyo ati chifukwa ili ku khoti.Chiradzulu Jameson Chausa adakanitsitsa kulankhulapo

“Nkhaniyi ilowanso ku bwalo la milandu Lolemba, ndipo dalaivalayu akadali m’manja mwa apolisi,” adalongosola Chausa.

Thumba, amachokera m’mudzi mwa Truwa, T/A Kadewere, m’bomalo.

Mkulu wa mgwirizano wa mabungwe a zaumoyo la Malawi Health Equity Network (Mhen) George Jobe adati zomwe adachita dalaivalayo zidali zosayenera komanso sakuyenera kupitiliza kugwira ntchito m’chipatala koma apite ku malo ena.

Iye adati ntchito yoyendetsa galimoto yonyamula odwala njofunika munthu wokhwima m’maganizo komanso wolemekeza odwala, choncho pakapezeka dalaivala wa khalidwe loipa, azimuchotsa msanga kuti asamaononge mbiri ya anzake.

“Pali woyendetsa galimoto zonyamula odwala ambiri omwe ali akhalidwe komanso mitima yabwino, takhala tikuwaona akuika miyoyo yawo pachiswe populumutsa odwala; mbiri ya awawa imaonongeka nawo chifukwa cha ochepa omwe alibe khalidwe,” adalongosola Jobe.

Iye adatinso zipatala zizikonza maphunziro a oyendetsa galimotozo pafupipafupi owaphunzitsa zina mwa ngodya za ntchito zawo.

Jobe adati bungwe lake limalandira madandaulo ochokera kwa anthu kudandaula ena mwa madalaivala a galimotozo monga dalaivala wina m’boma la Ntcheu, yemwe adasiya maliro panjira patatsala mtunda wapafupifupi makilomita atatu ndi komwe amakatulako ati chifukwa cha mafuta.

Iye adatsindika kuti madalaivala omwe akuona kuti sangakwanitse m’zipatala aziwasuntha n’kukawaika m’malo ena omwe angakwanitse.

“Koma tikupempha nkhani ngati izi kuti zisamafooketse madaivala omwe akugwira ntchito zawo bwino ndi mwachikondi,” adalongosola iye.

Avatar
Martha Chirambo
Previous Post

Sow the wind and reap a whirlwind

Next Post

Farmers get financial skills

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post

Farmers get financial skills

Opinions and Columns

Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

April 18, 2021
Political Uncensored

Mighty mess!

April 18, 2021
My Thought

Chakwera’s indecisiveness will be his downfall

April 18, 2021
People’s Tribunal

Cut the crap, act on abuse forthwith

April 17, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Minister of Labour Ken Kandodo

    Ministry defends ‘borrowing’ of Covid-19 funds

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera bites

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chilima in public projects inspection

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • ‘Tobacco is dying crop’

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Suspension without pay sparks debate

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.