Tuesday, March 2, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Zakudya za ziweto zasowa

by Bobby Kabango
01/10/2015
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

M’boma la Nsanje, ziweto monga ng’ombe, nkhosa ndi mbuzi zili pamoto chifukwa cha kusowa kwa chakudya.

Kwauma, ndipo tchire anthu atentha. Nthawi ngati imeneyi zaka zonse, ziweto akuti zimadalira kumtsinje wa Ruo komwe zimakadya bango, nsenjere ndi udzu wauwisi.cow

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Koma chaka chino chifukwa cha madzi osefukira, Ruo wabweretsa mchenga wambiri zomwe zachititsa kuti bango ndi udzu wauwisi ukwiririke. Mulibemo msipu ulionse.

Malinga ndi gulupu Manyowa, ziwetozi zikudalira makoko a chimanga, nthochi kapena zikonyo mwinanso mango.

“Ziweto zambiri zikumasonkhana pansi pa mitengo ya mango kuti anthu akamathyola zidyeko. Chifukwa cha kusowa chakudya, ziweto zambiri zaonda,” adatero Manyowa.

Koma alangizi amalangiza kuti zikatere alimi amayenera kuti azikhaliratu atapanga zakudya za ng’ombe ndi mbuzi kuti azizipatsa nthawi ngati ino.

Manyowa akuti m’mudzi mwake palibe munthu amene adapanga zakudyazo chifukwa cha mavuto a madzi amene adakumana nawo.

“Palibe amene adapanga zakudya za ziweto. Kodi mmene zidalili kuno ungamupeze munthu akupanga zakudya za ziweto? Mlimi aliyense adali ndi chiyembekezo kuti ziweto zizikadyera kumadzi monga zikhalira nthawi zonse osadziwa kuti kukhala mchenga wotere,” adaonjeza.

Mneneri mu unduna wa zamalimidwe, Hamilton Chimala, akuti alimi akuyenera kumakhala okonzeka ngati akufuna ziweto zawo zipulumuke nyengo ngati ino.

“Maiko ena ngakhalenso kwathu kuno timalangiza kuti alimi akuyenera kumakonza chakudya cha ziweto nthawi yotere isadafike. Zimanezi zimathandiza nthawi ngati ino. Yankho pa vutoli ndi lakuti alimi ayambe kupanga zakudya kuti ziweto zisakhale pamavuto,” adatero Chimala.n

Previous Post

Derby On

Next Post

Kamwendo secures loan move

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
Kamwendo: I am happy

Kamwendo secures loan move

Opinions and Columns

My Turn

Tackling global slowdowns

March 1, 2021
People’s Tribunal

Burglary at the hill

February 28, 2021
Search Within

Perseverance landed, is alive and well

February 28, 2021
Emily Mkamanga

Tasting your own salt in politics

February 28, 2021

Trending Stories

  • Olela: We are excited

    K5bn Sunbird Waterfront hotel opens May

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Lhomwe chiefs divided on paramount chief

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Experts fault IFMIS roll-out delays

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.