Friday, May 20, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Zigamulo zogwirira zikufooketsa

by Martha Chirambo
13/03/2021
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Sabata yatha inali imodzi mwa sabata yomwe inaika pa mbalambanda kuya kwa nkhani zogwiririra m’dziko muno. Pomwe bambo wina wa zaka 31 ku Zomba adagamulidwa zaka 21 pogwiririra khanda la miyezi inayi, bambo winanso wa zaka 50 ku Dowa adagamulidwa zaka 14 kundende pogwiririra mwana wa zaka 7. Nako ku Balaka bambo wa zaka 35 adapezekanso wolakwa pa mlandu wogwiririra ndi kupereka pathupi kwa mwana wa mchemwali wake wa zaka 15.

Mchitidwe wogwirira ukuoneka kuti ukuchulukira

Komatu omenyera ufulu wa ana sakukhutira ndi zigamulozi.

Desmond Mhango wa bungwe la NGO Coalition on Child Rights adati pali vuto lalikulu pa kagamulidwe ka anthu ogwirira ana ndipo zilango zomwe zikuperekedwa nzochepa komanso nzosapereka mantha kwa ena.

Malingana ndi Mhango mabwalo a milandu akufunika akhale ndi mlingo umodzi wa zigamulozi osati mlandu wofanana koma zigamulo zosiyana.

“Zikumachitika ndi zoti mlandu womwewo kwina apereka zaka 7, kwina zaka 14, palibe mlingo wofanana. Komanso uyu amugamula zaka 21 pogwirira khanda adzatuluka kundende khandali likadali ndi zaka zochepa ndipo akhonzanso kupereka chiopsezo pa moyo wake,” adalongosola Mhango.

Ndipo iye adanenetsa kuti zigamulozi ndi zokhumudwitsa ndipo adati bungwe lake likuunika njira zina monga kukasuma ku mabwalo amilandu akulu ngati sanakhutitsidwe ndi zigamulo.

Iye adati njira inanso ndi yoti mabungwe omenyera ufulu wa ana azikhala abwenzi a khoti pa nthawi ya mlandu kuti mwina zigamulo zizikhala zazikulu zikulu.

“Komanso nthawi zambiri ife a mabungwe timapereka nthawi yaikulu ku milandu ya m’matauni ndi m’mizinda poyerekeza ndi  milandu ya m’madera atali atali monga ku  Chitipa kapena ku Nsanje,” adadandaula motero Mhango.

Previous Post

DPP: House so divided

Next Post

Odds were against me, says Walter

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post
Hallmark, NBS Bank to host 
Country Club Monthly Mug

Odds were against me, says Walter

Opinions and Columns

Business Unpacked

Fixing economy needs action, not rhetoric

May 19, 2022
Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022

Trending Stories

  • CAF accepts FAM’s request on Flames fixture shift

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Onesimus leaves Major One Records

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MCTU pushes for 75% minimum wage hikeof

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Road traffic spot fines on way out

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mayors may face ballots

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.