Thursday, January 21, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Zikhulupiriro zina Zisokoneza mdulidwe

by Bobby Kabango
19/06/2016
in Chichewa, Editors Pick
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Zikhulupiriro zosiyanasiyana zikusokoneza ntchito ya mdulidwe wa abambo womwe unduna wa zaumoyo komanso mabungwe akulimbikitsa, Msangulutso wapeza.

RelatedHeadlines

Food imports doubled in 20 years—report

FAM ex-co approves women’s national league

Vendors back on streets amid Covid-19 surge

Ku Nsanje, Dowa komanso ku Nkhata Bay ndi maboma ena amene zikhulupirirozi zachititsa kuti abambo asamapite kuchipatala kukalandira mdulidwewu.

Malinga ndi Senior Chief Dzoole ya m’boma la Dowa, anthu ati samvetsa komwe kumapita kachikopa kamene adulako, zomwe zimawapatsa mantha.

“Anthu amaganiza kuti kachikopa kamene akadulako amakakachitira mankhwala. Maganizo awa ndi amene amachititsa anthu kuno kuti asapite kukalandira mdulidwe.

“Komanso anthu okwatira amaganiza kuti pamene akalandira mdulidwe, ndiye kuti akazi awo aziwayenda njomba chifukwa akawadula sangakakhale malo amodzi ndi mkazi wawo, ati panthawi iyi amaganiza kuti mkazi wawo akhoza kuawayenda njomba,” adatero Dzoole.

Mdulidwe wa abambo wakuchipatala ndi njira imodzi yothandiza kupewa kufala kwa HIV
Mdulidwe wa abambo wakuchipatala ndi njira imodzi yothandiza kupewa kufala kwa HIV

Dzoole adati m’dera lake, mwa amuna 10, amuna anayi okha ndi amene amalandira mdulidwe.

“Kampeni ili mkati moti mafumufe atiphunzitsa kuti timeme anthu akachititse mdulidwe, koma ndi amuna ochepa amene akupita kukalandira mdulidwe,” adatero Dzoole.

Senior Chief Kabunduli wa m’boma la Nkhata Bay wati kampeniyi yakanika kumeneko chifukwa anthu amaganiza kuti akakalandira mdulidwe ndiye kuti alowa chipembedzo cha Chisilamu.

“Ambiri kunoko amaganiza kuti amene alandira mdulidwe ndiye kuti ndi achipembedzo cha Chisilamu. Maganizo amenewa ndi amene akuchititsa kuti anthu asakhale nazo chidwi zokalandira mdulidwezo,” adatero Kabunduli.

Titafunsa mfumuyi ngati ikumemeza anthu ake kuti akachititse mdulidwe, iyo idati: “Ukawauza kuti kachitsitseni mdulidwe, akufunsa ngati iweyo unapanga. Ndiye ine pa msinkhu wangawu sindingapite kumdulidwe.

“Ndinetu munthu wamkulu, ndiye ndikakalandira mdulidwe lero, balalo lidzapola liti? …..sindingapange zimenezo komanso kampeni imeneyi ine sindikuchita nawo.”

Ku Nsanje, malinga ndi McKnowledge Tembo, HIV/Aids co-ordinator pachipatala cha boma, zikhulupiriro za anthu kumeneko zimati munthu akalandira mdulidwe ndiye kuti amaafooka kuchipinda.

“Kunoko tinaphunzitsa mafumu, amipingo ndi azaumoyo za ubwino wa mdulidwe, koma mukamayenda muja, anthu amafunsa zambiri zokhudza zikhulupiriro zawo ndi mdulidwe.

“Palibe amene adabwera poyera kudzatiuza kuti akufooka kuchipinda chifukwa walandira mdulidwe. Komabe anthu upeza akulankhula, ndi zabodza ndipo palibe umboni wake. Zoona zake nzoti macheza amakhalanso bwino m’banja mwamuna akakhala kuti adalandira mdulidwe,” adatero Tembo.

Nayenso Simeon Lijenje wa PSI akuti ndi bodza la mkunkhuniza kuti amuna amene alandira mdulidwe amafooka ndipo wati amuna amene adulidwa ndiwo amachitanso bwino  kuchipinda kusiyana ndi osadulidwa.

“Palibe umboni wa zomwe anthuwo akunena. Dziwani kuti mwamuna amene walandira mdulidwe ndiye amasangalala kuchipinda chifukwa amakwaniritsa bwino chilakolako cha mkazi wake,” adaphera mphongo Lijenje.

Iye adati kampeni ya mdulidwewu idayamba mu 2012 ndipo kuchokera mu October 2014 mpaka September 2015 pafupifupi abambo 93 642 ndiwo alandira mdulidwe m’bomalo.

Achipatala amati ngati abambo alandira mdulidwe, ndiye kuti pali mwayi woti chiwerengero cha anthu otenga kachilombo ka HIV podzera m’kugonana chingachepe ndi anthu 6 mwa 10 alionse (60%), malinga ndi mabungwe a WHO komanso UNAIDS.

Kuyambira mu 2007, mabungwewa akhala akubwekera kuti mdulidwe umathandize kwambiri kuti kachilomboka kasafale kwambiri.

Malinga ndi mabungwewa, maiko 14 a kummwera kwa Afrika komanso kummawa, ndiwo ali kalikiriki kupangitsa kampeni kuti amuna azikalandira mdulidwe.

“Mdulidwe wa abambo ndi pamene achipatala amadula kachikopa kakutsogolo kwa chida cha abambo. Kachikopaka kamasunga zoipa, koma ngati walandira mdulidwe, amakhala waukhondo. Zoipazo zimakhala zasowa malo oti zisungidwenso,” lidatero lipoti la UNAids, nkuonjera kuti mdulidwe umathandiza kuchepetsa matenda a khansa ya khomo la chiberekero cha amayi.

Previous Post

Church raises funds for bus

Next Post

Brother Dostie: The educator, mentor who loves Malawi

Related Posts

Malawi has been importing maize over the years largely due to floods that have impacted output
Business News

Food imports doubled in 20 years—report

January 21, 2021
DD Sunshine (in blue) taking on Blantyre Zero during the national championship early this year
National Sports

FAM ex-co approves women’s national league

January 21, 2021
Vendors line up in Blantyre at old Nandos
National News

Vendors back on streets amid Covid-19 surge

January 21, 2021
Next Post
Bro Dostie admires a medal of recognition Chiku Kalilombe 
presented to him on behalf of the ‘Box 2’ alumni

Brother Dostie: The educator, mentor who loves Malawi

Trending Stories

  • Escaped South African bail: Bushiris

    Bushiri says not seeking political intervention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty US deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 initiative raises K18.3m in 2 days

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Vendors back on streets amid Covid-19 surge

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.