Wednesday, January 27, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Zinthu zitatu mu nkhuku imodzi ya Mikolongwe

by ESMIE KOMWA
20/04/2019
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Katswiri wa ulimi wa ziweto wa ku Lilongwe University of Agriculture and Natural Resources (Luanar) Timothy Gondwe wati kukhala ndi nkhuku ya Mikolongwe imodzi ndi chimodzimodzi kukhala ndi nkhuku zitatu—yanyama, yachikuda ndi yamazira.

chickens 1 | The Nation Online
Nkhuku ya Mikolongwe imafika makilogalamu 4.5

Iye adati nkhuku ya Mikolongwe imakula kwambiri, imaikira mazira ambiri, komanso kukoma kwa mazira ndi nyama yake ndi chimodzimodzi nyama ndi mazira a nkhuku yachikuda.

RelatedHeadlines

Amapita kukagula zomwera tiyi

Anatchezera

Odzipha akuchuluka

“Nkhuku ya Mikolongwe imakula kwambiri  moti tambala mpaka amafika makilogalamu 4.5 pamene thazi amatha kulemera makilogalamu 4 pa miyezi 4 kapena 6 yokha.

“Pachaka nkhuku ya Mikolongwe imaikira mazira apakati pa 200 ndi 250,” adatero Gondwe.

Kuonjezera apo, katswiriyu adati mlimi atha kukwatitsa anapiye ake ndi a nkhuku zachikuda kuti akhale nkhuku zolimba komanso zopirira ku matenda.

Gondwe adati ichi n’chifukwa chake nkhukuzi zikhoza kuwetedwa kumudzi ndikumabweretsa phindu lochuluka.

Malingana ndi katswiriyu, nkhuku zokwatitsazi zimakula ndi kuikira mazira ambiri oposa azachikuda.

“Mazira ake amaposa a nkhuku zachikuda ndi magawo a pakati pa 20 ndi 30 pa 100 aliwonse ndipo zimatha kuikira okwana 200 pachaka,” iye adatero.

Gondwe adati izi zimathandiza mlimi kupeza nyama yochuluka ndi mazira ambiri choncho ndalama, komanso ndiwo sizisowa pakhomo.

Mlangizi wa ziweto wa ku Blantyre Agriculture Development Division (Bladd) John Pirate Kothowa adati ngakhale nkhukuzi zimakula, komanso kuiikira mazira ochuluka n’zosiyana kwambiri ndi zachikuda m’chikhalidwe chake.

Iye adati ichi n’chifukwa chake zimatha kumayenda  n’kumadzitolera zokha chakudya.

“Chifukwa choti zimatenga nthawi yotalikirapo kuti zikule, kuziweta ngati zachizungu pomazidyetsa chakudya chogula n’kudzichepetsera phindu,” adatero Kothowa.

Gondwe adati alimi akumidzi akhoza kuweta nkhukuzi ngati momwe amawetera  zachikuda, koma zimafunika kumazipatsa chakudya choonjezera  m’mawa, masana ndi madzulo.

Iye adati chakudyachi ndi monga gaga wothira mchere pang’ono ndipo ngati pali zakudya zina za m’gulu la nyemba, azisakanizako gawo limodzi mwa magawo atatu aliwonse.

Katswiriyu adafotokoza kuti mlimi aziika chakudyachi pafupi ndi khola kapena pamene nkhuku zimakonda kudutsapo zikamapita kukadya.

“Pambali pa chakudya pazikhala madzi akumwa aukhondo kuti zizimwa momwe zafunira.

“Mlimi azitsatira dongosolo lonse la katemera wa chitopa kuti zikhale zotetezeka,” iye adatero.

Gondwe adafotokoza kuti khola lizikhala lotakasuka, louma, lolowa bwino mpweya  ndipo ngati n’kotheka la m’mwamba chifukwa ndi lomwe nkhuku zoyendayenda zimakonda.

Katswiriyu adafotokoza kuti alimi am’tauni omwe amatha kupeza mwayi oweta nkhuku zokwatitsa, akhoza kumazipatsa chakudya chopanga okha kapena chogula cha nkhuku za mazira, koma chizingokhala choonjezera chabe.

Iye adati izi zili choncho chifukwa nkhuku za Mikolongwe zimadana ndikutsekeredwa m’khola.

Lastseen Jonamusi ndi m’modzi mwa alimi a nkhuku za Mikolongwe mu mzinda wa Blantyre wayamikira ulimiwu kuti ndi wabwino.

Iye adati adayamba kuweta mu December chaka chatha koma padakali pano zakula kale.

“Pano maso ali kunjira kudikirira tsiku lomwe ziyambe kuikira mazira kuti ndiyambe kudyerera,” adabwekera motere mlimiyu.

Previous Post

Lule adachita chokong’ontha

Next Post

Akuti akukumana Ndi womwalira

Related Posts

marriage | The Nation Online
Chichewa

Amapita kukagula zomwera tiyi

January 3, 2021
Chichewa

Anatchezera

January 3, 2021
An illustration of court proceedings
Chichewa

Odzipha akuchuluka

January 3, 2021
Next Post
fire | The Nation Online

Akuti akukumana Ndi womwalira

Trending Stories

  • Mlusu presents the budget in this file photo

    Budget off rails

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • SA returnees in forced quarantine

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • New mashup draws mixed reactions

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Donors up game in Covid-19 fight

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Spread hope not fear

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Turn

When schools become inaccessible, a glimmer of hope in a coding boot-camp

January 27, 2021
My Turn

Behaviour change key in Covid-19 fight

January 25, 2021
Emily Mkamanga

Citizens power brings change

January 24, 2021
Search Within

The rural farmer needs to take centre stage

January 24, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.