Saturday, February 27, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Zochitika m’minibasi

by Tadeyo
15/11/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Tsikulo pa Wenela padalibe zomvera nyimbo. Nanga abale anzanga, anthu akuluakulu ngati ife tingamamvere nyimbo monga Tsika Msungwana Tsika? Nanga inu mungamvere nyimbo ija ya Msati Mseke. Za nyimbo imeneyi ndidamva kwa Gervazzio, amene akuti sangayerekeze kuika pamalo paja timakonda pa Wenela.

Amavala zigoba….Amadzipaka matope….

RelatedHeadlines

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

“Uku ndiye timati kufwala gule, kuulula vilombo. Adamuuza ndani kuti amachita kuvala? Kukadakhala kwathu ku Thiwi ku Nkhotakota, tikadacheza mwana uyu,” adatero Gervazzio.

art

Tsono tsiku limenelo kudali kuonera mafilimu a ku Nigeria. Pajatu ine mafilimu amenewa ndidaimika manja kalekale kuti sindidzaoneranso, amataitsa nthawi. Zoona filimu izikhala yoonetsa munthu akuliza galimoto, kudzaponda kuti vruuuu! Kenako kuyamba kuitana wapageti kuti akatsegule. Akatero wageti kulimbana ndi geti…. Kenako ndiye kuti muonera mphindi zisanu mkuluyo akuyendetsa galimoto….

Koma filimu imene tinkaonera tsikulo ndiyo yandichititsa kuti ndilekeretu kuonera filimuzi. Ngakhale wina atandithira Doom mkamwa, sindingachite. M’filimuyo mkazi wina adafuna kupha mwamuna wake kuti atenge chuma chake. Iye adaphika chakudya ndipo adathiramo tameki. Kuti adziwe kuti tamekiyo wakolera mayiyo adalawa chakudyacho!

Tsiku lotsatira, wa minibasi ina adati akufuna agwire ntchito ina ndipo adandipempha kuti ndiyendetse mmalo mwake. Ndidaima pa Wenela uku wina akuitanira. “Ndirande! Ndirande! Ndirande awiri a chamba! Awiri a change muno ku Ndirande!” adali kutero.

Nthawiyo nkuti ndikukhoma marivesi, kudzapititsa patsogolo pang’ono.

Mpando woyandikana ndi ine padakhala mkulu wina ndipo kuchitseko kudali msungwana wina amene anali ndi foni yake m’manja. Iye adali ndi chikwama chija amachitcha mwina ndi wokagona pamiyendo pake.

Chomwe chinkandichititsa chidwi chidali chakuti bamboo uja ankasunzumira zomwe msungwana amalemba pafonipo. Pena mzibamboyo amaseka nawo nkhani za msungwanayo. Ndikhulupirira idali Whatsapp imeneyo.

Mtsikana uja adaoneka kuti amanyansidwa ndi zochita za bamboo uja. Bamboyo adali kunjoya zolemba za msungwana uja.

Kenako, tikuyandikira pa Chimsewu mzibambo uja adayamba kukuwa. “Njoka! Njoka! Njoka!” adadumpha ndipo adachititsa kuti ndisiye chiwongolero. Pomwe ndimadzachigwiranso, nkuti minibasi ikutaya msewu.

“Mayo ine ngozi iyi! Ngozi iyi!” ena adali kukuwa.

“In the name of Jesus! In the name of Jesus!” enanso adali kukuwa.

Mwa chisomo, ndidakwanitsa kuimitsa minibasi ija. Padalibe wovulala. Koma bamboo uja adatsegula chitseko ngakhale adali pakati. Adamudumpha mstikana uja nkutuluka panja.

Adali kukuwa: “Njoka! Njoka! M’chikwama! Njoka!”

Msungwana uja adali kuseka chikhakhali.

“Bamboyu amawerenga mauthenga anga, ndiye ndimafuna asiye kuwerenga mauthenga a eni. Ndinangolemba uthenga uwu,” adatero akundiwerengetsa uthenga wopita kwa bwenzi lakewo.

Ndili m’minibasi koma abambo ndayandikana nawo akungowerenga mauthenga anga. Sakudziwa m’chikwamamu muli njoka.

Gwira bango! Upita ndi madzi!n

Previous Post

Lambani wadza ndi Knock Out

Next Post

UN ponders over MDF troops Burundi deployment

Related Posts

HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Next Post
still barred from his ministerial duties

UN ponders over MDF troops Burundi deployment

Opinions and Columns

My Diary

Light that came with Covid-19

February 27, 2021
Guest Spot

Resurgence of albino killings deplorable

February 27, 2021
Back Bencher

Is violence a boomerang effect in DPP?

February 27, 2021
Off the Shelf

Sacrificial lambs of a dysfunctional system

February 27, 2021

Trending Stories

  • Chiyembekeza (L) and Kusamba Dzonzi during the briefing

    Admarc secures K430bn to revamp operations

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Censorship Board acts on ‘Aunt Nellie’ videos

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Grace Chinga makes posthumous return

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mlusu in tight spot on budget

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Dodma wants Covid-19 funds back from councils

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.