Thursday, January 21, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Zotsamwitsa pa kutseguliranso sukulu

by Steven Pembamoyo
05/09/2020
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pomwe ana asukulu akuyembekezera kutsegulira sukulu, aphunzitsi akuti sadakonzeke zokaphunzitsa chifukwa boma silikuonetsa chidwi pa nkhawa zawo.

Mlembi wa bungwe la aphunzitsi la Teachers Union of Malawi (TUM) Charles Kumchenga wati aphunzitsi adapereka nkhawa zoti boma liwapangire sukulu zisadatsegulidwe koma mpaka lero palibe chomwe chikuoneka.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Kumchenga | The Nation Online
Kumchenga: Aphunzitsi adadandaula

Izi zikusemphana ndi zomwe mlembi wamkulu wa unduna wazamaphunziro Chikondano Musa wanena kuti undunawo wankonzeka mokwanira.

Koma kadaulo pa zamaphunziro Benedicto Kondowe wati mbali ziwirizi zipereke chithunzithunzi choyenera kwa Amalawi chifukwa njomba zikhoza kusokoneza makolo.

Makolo ena adandaula kale kuti kutsegulidwa kwa sukulu kwawapatsa chipsinjo chifukwa adali osakonzeka moti ngati boma silipeleka nthawi yokwanira yoperekera fizi, ana ambiri sapita.

“Apa ndalama yavuta kale ndi Covid-19, kupatula apo, atidzidzimutsa ndalama tilibe komabe tiyesetsa kukwereta kuti ana apite kusukulu,” watero Margaret Ausi wa ku Salima.

Bungwe la TUM lati lidagwirizana ndi boma kuti aphunzitsi apatsidwe ndalama zaukadziotche komanso maphunziro apadera ophunzitsira m’nyengo ya Covid-19.

“Potseka sukulu adati akuwopa kuti kusukulu kungafalitse Covid-19 kutanthauza kuti kusukulu n’koopsa ndiye pakufunika ndalama yaukadziotche,” watero Kumchenga.

Lachiwiri lapitali aphunzitsi adawopseza kuti ngati sapatsidwa ndalama yaukadziwotche, sayamba kuphunzitsa chifukwa nawo ndi anthu.

“Tikusiyana pati ndi ogwira ntchito kuchipatala ndi kupolisi omwe amalandira ndalama yaukadziwotche? Nafeso atipatse,” adatero aphunzitsi mukalata yomwe adapeleka ku unduna wa zamaphunziro.

Koma nduna yazamaphunziro Agness Nyalonje wati zonse zili mmalo sukulu zitsegulidwa Lolembali ndipo wati makolo atumize ana kusukulu.

“Sitingangobwera n’kumati tikutsegulira sukulu, takonzeka moti makolo atumize ana kusukulu,” watero Nyalonje.

Boma lidatseka sukulu pa 23 March 2020 malipoti oti Covid-19 yafika ku Malawi ndipo ana asukulu akhala pa tchuthi chosakonzekera kwa miyezi isanu.

Panyengoyi, ana ambiri makamaka asungwana atenga pathupi ndi kukwatiwa some zikutanthauza kuti maphunziro a ana oterewa asokonezeka.

Chiwerengero cha anthu opezeka ndi Covid-19 chidakwera kwambiri m’miyezi ya June ndi July koma pano chiwerengerocho chayamba kutsika ndipo boma lati likukhulupilira kuti Covid-19 itha.

Previous Post

‘It’s our time to eat’

Next Post

Alimi alirira Admarc

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
People queue to buy maize at Admarc market

Alimi alirira Admarc

Trending Stories

  • Escaped South African bail: Bushiris

    Bushiri says not seeking political intervention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty US deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Vendors back on streets amid Covid-19 surge

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 initiative raises K18.3m in 2 days

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.