Tuesday, January 19, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Zovula pa Wenela ayi, tamva!

by Tadeyo
26/06/2016
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Tsikulo pa Wenela padali ziii! Moti ojiya, osolola ndi osenza onse adali khumakhuma. Ndalamatu ndalama zalowa ku silent ndiye anthu sakuyenda.

RelatedHeadlines

Amapita kukagula zomwera tiyi

Anatchezera

Odzipha akuchuluka

Basi ya Lilongwe imatenga tsiku lonse kuti idzadze. Ambirinso amachita kunenera.  Nchifukwa chake ndidangoganiza zolowera malo aja timakonda pa Wenela. Ndidakapeza Abiti Patuma ndi Gervazzio akumvera nyimbo ya Lucius.

Poti sitima, imaphweka akamayendetsa wina….

Sindikudziwa kuti nyimboyo adayiika chifukwa chiyani!

Abiti Patuma adali bize pafoni yake.

artrt

“Koma abale, phungu uyunso ndiye amangokhalira pa Facebook. Taonani lero akuti iye sakufuna kukwezeredwa ndalama. Ndidakuuzani kale kuti uyu wokonda kuvina kanindoyu amangofuna kuti anthu azimumvera.

“Mwaiwala zija ankanena zolodza azungu osakaza la Mulanje phiri; mwamuiwala kuti ngwa nthabwala basi?” adatero Abiti Patuma.

“Zoona. Amati avula, ayende tauni ya Lilongwe onse aone kuti iye ndi munthu wamkulu, wotamba masana likuswa mtengo! Chomwe ndikudabwa nchakuti kodi bwanji phunguyu amachita zosiyana ndi aphungu ena?

“Akamabwera ku Nyumba ya Malamulo amakwera Bajaj, inde galimoto kaya ndi njinga ya matheyala atatu? Saona anzake akayenda pa galimoto zopuma ngati olemekezeka? Uyutu uyu kupanda kusamala naye adzalaula ndi pa Wenela pano!”

Adayankhira Gervazzio: “Ndikuona ngati nzeru zikumuchepera ameneyu, mwina zamuchulukira kwambiri?”

Abale anzanga, kunena zoona wamisala adaonadi nkhondo!

Posakhalitsa tindangoona  uyo watulukira atavala mwado wofiira wopanda lisani. Kumtundaku malayanso ofiira koma odula mikono. Tsinya lili gaa pankhope. Kenaka adayambitsa nyimbo, amvekere: Zivute, zitani ife Amalawi…!

Chigulu chidali chitasonkhana kuti chione munthu adalonjeza kuti avula uja, chidayankhira: Tili pambuyo pa maalubinoo!

Kenaka tidamva ali Left! Right! Left! Right…

Wayambika wa ndawala! Kuguba ulendo wa ku Nyumba ya Malamulo.

“Indetu ndinena ndi inu aphungu anzanga. Dziko lafika pena. Lamulo ligwire ntchito. Diso kwa diso, mphuno kwa mphuno! Akakumenya mbali inayi, nawenso menya! Tatopa ndi ulemu…Ndiponso a AI, fokofu, akagwere ku Gahena! Asaa! Ati tisaphe wopha alubino, zamkutu!”

Musandifunse kuti a AI ndani, poti nane sindikuwadziwa ndipo olo nditawadziwa sindingakuuzeni. Nanga ndichite kukuuzani kuti ndi aja, aja adabwera aja, kodi mumati andani paja?

Kenaka munthu adavala mwado uja adayamba kulira ngati mwana! Palibe adaseka. Ndidayang’ana Abiti Patuma…nawonso adagwetsa tsozi!

Gwira bango, upita ndi madzi mwaiwe! n

Previous Post

Tracing theology and place of music in worship

Next Post

Kodi Chipuwa wabwerera kumalonda?

Related Posts

marriage | The Nation Online
Chichewa

Amapita kukagula zomwera tiyi

January 3, 2021
Chichewa

Anatchezera

January 3, 2021
An illustration of court proceedings
Chichewa

Odzipha akuchuluka

January 3, 2021
Next Post
Chipuwa: I am nursing injury

Kodi Chipuwa wabwerera kumalonda?

Trending Stories

  • Not yet given retirement benefits: Mutharika

    Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Wasteful Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Laz Chakwera’s Covid-19 strategy

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • HRDC takes govt to task over Covid-19 strategy

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Neef bosses, board fight in court

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
Political Uncensored

Maddening chaotic virus

January 17, 2021
Emily Mkamanga

Chakwera has to instill unity

January 17, 2021
People’s Tribunal

Perilous times and the need for accountability

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.