Thursday, February 25, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

‘Zulani mitengo ya fodya poopetsa matenda’

by Dailes Banda
10/10/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Nthawi ino alimi ambiri a fodya ali kalikiriki kufunafuna mbewu, kukonza malo omwe adzalimepo komanso kukonza ndi kufesa nazale.

RelatedHeadlines

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

Aphungu akumana lolemba

Ndi ana omwe akudzipha

Ngakhale izi zili choncho alimi ena m’maboma a Mzimba ndi Rumphi akutsalira pantchitoyi kaamba koti iwo sadazulebe mitengo ya fodya m’minda mwawo.

For better tobacco production, quality seeds are vital

Mlangizi wa za ulimi Lewick Zimba wauza Uchikumbe kuti izi zikhoza kudzaononga fodya munyengo ikubwerayi.

“Alimi amayenera kuzula ndi kuotcha mitengo imeneyi akangomaliza kuthyola fodya wawo kuti aphe tizilombo tonse tomwe tingakhale mumitengoyo.

“Fodya ali gulu limodzi ndi tomato ndi mbewu zina zomwe sizichedwa kugwidwa ndi matenda ndipo mitengo ija ikasiyidwa kwa nthawi yaitali m’munda umasanduka malo omwe tizilombo timasweranamo,”adatero Zimba.

Zimba adati madera amasiyana nyengo yokolola fodya. “Madera a kummwera ndi pakati amayenera kuyambirira kuzula pomwe madera a kumpoto amamalizira ngakhale nthawi yake madera onsewa ndi miyezi ya March mpaka April,” adatero Zimba.

Iye adati alimi omwe sadazule ndi kuotcha mitengo ya fodya m’minda mwawo akuyenra kutero nthawi ino ngati akufuna kudzapindula ndi fodya wawo nyengo ikudzayi.

“Fodya amafunika chisamaliro chokwanira ndipo chisamaliro chimenechi chimayamba mlimi akangokolola fodya wake m’munda,” adatero Zimba.

Iye adati alimi akuyenera kuzindikira zomwe akuyenera kuchita ndi nthawi yomwe akuyenera kutero kupewa kulakwitsa kapena kusokoneza zomwe zikadatha kupeweka.

“Alimi akuyenera kumvera alangizi komanso ngati apali zinthu zomwe sakumvetsetsa akuyenera kufunsa kwa alingizi a kudera lawo,” iye adatero.

Mlangiziyu adati Malawi ndi dziko lomwe limadalira ulimi wa fodya pobweretsa ndalama za kumaiko akunja kotero n’kofunika kuti fodya azisamalidwa bwino kuti phindu lake lizioneka pokhala kuti mbewuyi imafuna ntchito yambiri.

Amon Gondwe, mmodzi mwa alimi amene mpaka pano sanazulebe mitengo ya fodya m’boma la Rumphi, wati ntchito imawakulira kuti ayambe kuzula nthawi yomwe amaliza kuthyola fodya.

“Timati tidzazulabe kenaka mpaka kumapezeka kuti nthaka yauma ndipo mitengoyi imalimba ndiye timangozisiya,” adatero Gondwe.

Iye adati akudziwa za ubwino wozula mitego ya fodyayo akangomaliza kukolola, makamaka potengera kuti ntchito imachepa, koma kwina kumakhala kutayirira kumbali ya alimi, amene ambiri mwa iwo amafuna “adzipepese” kaye akangogulitsa fodya wawo.

Previous Post

Children with hearing impairments shine

Next Post

Mzuzu vendors defy council

Related Posts

Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Parliament in session
Nkhani

Aphungu akumana lolemba

February 19, 2021
An illustration of court proceedings
Chichewa

Ndi ana omwe akudzipha

February 14, 2021
Next Post
The market was laid to waste by fires twice this  week

Mzuzu vendors defy council

Opinions and Columns

In pursuit of development

The Chinese approach to network-building

February 25, 2021
Business Unpacked

Back to the drawing board on budget

February 25, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

February 25, 2021
My Thought

Malawi needs fixing, not politicking

February 21, 2021

Trending Stories

  • Co-chaired the task force: Phuka (L) and Mwanamvekha

    K780M Dodma Covid-19 feast

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Bushiri’s daughters blocked from flying out

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Censorship Board acts on ‘Aunt Nellie’ videos

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Convention In July 2023—DPP

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside k6.2bn

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.