Monday, May 16, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Agulitsa mwana ndi K18 miliyoni

by Martha Chirambo
26/02/2022
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Nkhondo ndi anansi. Wodya naye mbale imodzi ndiye amakupereka kwa adani. Izi zapherezera kwa mwana wina wa zaka 11 yemwe msuweni wake anamutsatsa pa mtengo wa K18 miliyoni.

A Madalitso Wyson, yemwe ali ndi zaka 22, adapita kusukulu kwa mwanayu ku Chingazi, m’dera la Ntambanyama m’boma la Thyolo pa nthawi yopuma ndi kumutenga mwanayo. Apolisi m’boma la Thyolo atsimikiza za nkhaniyi.

Malinga ndi mneneri wa polisi m’bomalo a Amos Tione, a Wyson atamutenga mwanayo yemwe ali m’sitandade 2, adapita naye kwa chibwenzi chake komwe anakagona kwa tsiku limodzi.

“Zonsezi zimachitika makolo a mwanayo asakudziwa kanthu,” anatero Tione.

Iwo adati kutacha m’mawa, Wyson adamutenga mwanayo kupita naye pamsika wa Ntambanyama pomwe anakakumana ndi sing’anga wina ndi kumutsatsa malondawo.

“Koma sing’angayo anatsina khutu anthu ena komanso apolisi ndipo a Wyson adatsekeredwa pamlandu wozembetsa ana mosemphana ndi gawo 15 la malamulo wozembetsa anthu,” adatero a Tione.

Msangulutso udacheza ndi sing’anga Billy yemwe anati zokambirana zake ndi Wyson zidaonetsa kuti munthu yemwe mnyamatayo anapangana naye kugula mwanayo anamugwiritsa fuwa lamoto.

Billy adati Wyson atafika pamalo ake a ntchito anamuitanira pambali n’kumuuza kuti pali bizinesi ya mwanayo.

“Adandiuza kuti adapangakonso bizinesiyi mmbuyomo ndi anzake omwe adamupusitsa ndi kuthawa ndi ndalama, ndipo ulendo uno adaganiza zochita bizinesiyo yekha,” adatero a Billy.

Iwo adati Wyson adawauzanso kuti ngati akufuna akhoza kumupatsa wokonzakonza.

“Pofuna kupulumutsa moyo wa mwanayo, ndidamuyenda pansi ndi kupeza mkulu wina yemwe adanamizira ngati wogula kwinaku ndikuimbira foni apolisi omwe adadzamumanga,” adatero a Billy.

Iwo adati aka si koyamba chifukwa mmbuyomu adafikiridwakonso ndi anthu ena omwe adawauza kuti akufuna chizude pa mtengo wa K10 miliyoni ndipo adazindikira kuti iyi inali njira yongozembaitsa chifukwa anthuwo amafuna munthu.

Ndipo mkulu woyang’anira maphunziro m’boma la Thyolo a Godfrey Kubwense adatsimikiza kuti mphunzitsi wamkulu wa pasukulu ya Chingazi adawadziwitsa za nkhani ya mwanayo.

Nkhani zozembetsa anthu zakhala zikukula m’dziko muno. M’chaka cha 2020 anthu 688 adapulumutsidwa ku mchitidwewu.

Previous Post

Elizabeth Bandason: Shaping the future of farming with science

Next Post

Players union faults Bullets over contracts

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post
Nyirenda: The door
is open

Players union faults Bullets over contracts

Opinions and Columns

Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022
My Thought

Two years of nothing but development rallies

May 15, 2022

Trending Stories

  • Chakaka-Nyirenda: The DPP will look into it

    Embassy assets sold, money untraceable

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • PAC clears Macra director general, cautions board

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse cracks suspicions grow

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Two years of nothing but development rallies

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • My wife is a WhatsApp addict

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.