Wednesday, June 29, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

by Martha Chirambo
22/05/2022
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Abambo ena 8 adabwitsa anthu ku Chibavi, mumzinda wa Mzuzu atapezeka ndi yunifomu zapolisi.

Zovalazi ndi monga zigoba zovala panthawi ya zionetsero komanso za mphepo zolembedwa Malawi Police.

Ena mwa amene akuwaganizira kuti adaba katundu wapolisi ku Mzuzu

Pomwe Msangulutso unayendera kumalo komwe abambowo adagwidwa, anthu oyandikana nawo nyumba anati zachitikazo zawapatsa mantha.

Mmodzi mwa anthuwo a Madalitso Mzumara adati samadziwa kuti akukhala limodzi ndi anthu omwe akusunga katundu wa apolisi.

“Zatiopsa, ngati anakwanitsa kupeza zovala za apolisi ndiye kuti ifenso akanatha kutichita chipongwe,” anatero Mzumara.

Iwo anati izi zizichititsa kuti anthu azikaikira akaona apolisi ngati alidi achilungamo kapena onyenga.

Polankhulapo mneneri wa apolisi ku Mzuzu a Paul Tembo adatsimikiza kuti a Thomson Mbewe, a Chikondi Malinga, a Ramsey Chirwa, a Famous Nsani, a Jeremiah Banda, a Ladson Banda, a Alex Kavenji and a Gerald Mwale apezeka ndi yunifomu ya apolisi.

A Tembo adati anthuwo akuwaganizira kuti ndi omwe amasowetsa mtendere ku Chibavi.

“Anthuwa tawatsegulira mlandu wopezeka ndi katundu wakuba ndipo awonekera kubwalo la milandu masiku akubwerawa,” anatero a Tembo.

Iwo adati anthu akufuna kwabwino ndiwo adawatsina khutu apolisi kuti anthuwo ali ndi yunifomu za polisi.

Izi zachitika pomwe chitetezo chalowa pansi m’dziko muno ndipo ambiri akuloza zala apolisi kuti sakuchita zotheka pobwezeretsa chitetezo.

Nkhaniyi ili m’kamwa m’kamwa mwa Amalawi, bomba linanso laphulika kundende ya Chichiri komwe munthu wina anadzizimbaitsa ngati wapolisi n’kukatulutsa mkaidi kundendeko.

Nkhaniyi ikuti munthuyo anamutenga m’kaidiyo ponama kuti akupita naye kubwalo la milandu.

Ndipo mneneri wa ndende m’dziko muno a Chimwemwe Shaba kuti nthambi ya ndende ikufufuza za nkhaniyi komanso kufufuza komwe awiriwo adalowera.

Ndipo mphunzitsi wa za chitetezo pa sukulu ya Mzuzu University a Aubrey Kabisala anati kupezeka ndi yunifomu zapolisi kukutanthauza kuti anthuwo ali ndi cholinga chomadzizimbaitsa ngati apolisi.

Iwo adati izi zikutanthauza kuti ukadaulo wa umbanda ndi umbava wafika pa mlingo wina chifukwa azichita moonetsera moti anthu sangadziwe kuti ndi mbava mwachitsanzo: pomaima pamsewu kuimitsa galimoto, kumapita m’midzi yakutali kukalanda katundu podzizimbaitsa ngati apolisi.

“Akhoza kupita m’misika yakutali ngati apolisi oyenda mongoyerekeza ndi bungwe lotolera misonkho la Malawi Revenue Authority(MRA) n’kulanda anthu katundu kumeneko, anthuwo mosadziwa n’kumati ndi apolisi. Apapa tingoti anthuwo ali n’kuthekera kogwira ntchito ngati apolisi amene,” anatero a Kabisala.

Iwo analangiza apolisi kuti mpofunika kuphunzitsa anthu mwakathithi kupempha kuona chiphaso cha wapolisi kapena kufunsa nambala yake ya kuntchito kuti azitsimikizadi ngati ali wapolisi.

“Vuto ndi loti ambirife timakhala ndi mantha, timaopa kuti apolisiwo ationa ngati ndife achipongwe ndipo tikumana ndi mavuto,” iwo adatero.

Apa a Kabisala adatinso anthu akhozanso kupempha apolisi omwe akuwakaikira kuti ngati pali milandu akakambire kusiteshoni ya polisi pofuna kudziteteza ku mbava zodzizimbaitsa ngati apolisi.

Previous Post

Hazel Mak: Award winning musician, feminist

Next Post

Malawi overlooks players diet

Related Posts

Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Katundu wa a Mtambo adali kuseri kwa ofesi za khonsolo
Nkhani

Agona ku maofesi a khonsolo ya Mzuzu

June 4, 2022
Nkhani

Woimba abedwa mumzinda wa mzuzu

May 28, 2022
Next Post

Malawi overlooks players diet

Discussion about this post

Opinions and Columns

My Turn

US court threatens women’s rights

June 29, 2022
People’s Tribunal

Two years later and we are still singing same song

June 26, 2022
Big Man Wamkulu

Wife’s relatives have taken over my house

June 26, 2022
My Thought

Stop cyber harassment

June 26, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • ACB cleared Sattar contract—Documents

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Britain squeezes Zuneth Sattar

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MET says cold, wet weather will continue

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mwanamvekha wants his case dismissed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K243bn Malawi trade deal on rocks

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.