Tuesday, April 20, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Anatchereza

by ANATCHEZERA
18/10/2020
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Agogo ndili ndi zibwenzi ziwiri koma onsewo ndi pachibale komanso amadziwana. Ndikawauza kuti andisiye onse amakana, nditani gogo chifukwa onse kwathu amabwera koma zundivuta kuthananazo?

Nkhani yanu ikutipatsa mafunso ambiri. Tikukhulupirira kuti amuna onsewo sadakufunsireni tsiku limodzi. Zikuonetseratu kuti aliyense adabwera payekha. Ndiye mutalola woyambayo, n’chifukwa chiyani mumalolanso wachiwiri yemwenso ndi mbale wa woyambayo? Izitu ndi zomwe mumafuna. Ngati mukufuna kuti akusiyeni, lekani kuwayendera, kuwayankha mafoni awo ndipo muchotse nambala zawo m’foni yanu. Musalole kuti afike pakhomo pano ndipo asiya. 

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Ndine VM ndimachokera ku Mulanje ndili ndi akazi atatu, ndidapezeka ndi akazi atatu chifukwa enawa amkandikonda kumayambiriro achikondi, kenako amayamba kupanga zofuna zawo. Ndiye panopa wina ali ndi mwana wa mng’ono, wina ndi woyembekezera komanso wina alibe mwana. Panopa onsewo ali payekhapayekha. Amawerengera kuti ali ndi mwamuna kunena ine, ndipo kwa ine onsewa ndimawaona chimodzimodzi, ndiye ine zikundivuta kusankha chonde thandizeni kodi ndisankhe uti? Onsewa akufanana zochitika zawo.

Bambo VM,

Penapake ndikuvutika kumvetsa chimene chidakupangitsani kuti mpaka mukhale ndi akazi atatu. Woyamba wakanika kupereka chikondi, wachiwirinso mpaka kukhala ndi wachitatu? Zovuta kumvetsa komabe muyenera kutenga amene ali ndi mwanayo. Ameneyo ndi woyamba enawo amupeza komanso kuli mwana amene akufunika chisamaliro chanu. Wachiwiriyo mudzitumiza thandizo kuti asamalire mimba ndipo mudzathandizebe mwana akadzabadwa. Wachitatuyo aone msana wanjira.

Ndine mnyamata wa zaka 29, ndidapanga chibwenzi ku Mangochi koma mkaziyo akukana kuti ndikaonekere kwawo.

Ndine C ku Thyolo.

Achimwene a C, chibwenzi nthawi zambiri chimakhala ndi ganizo limodzi kuti mawa mudzamange banja. Ameneyo banja sakulifuna chifukwa achikhala amalifuna bwezi atakhala woyamba kukuitana kuti ukaonekere. Uyu asakutaitseni nthawi, mulekeni azipita. 

Chibwenzi changa chimandikaikira chifukwa amandigwira ndi ma message a zibwenzi zanga zakale. Nditani kuti adzindikhulupirira ine

T ku Zomba.

T,

Palibe munthu amene angakukhulupirire ngati ukuchezabe ndi zibwenzi zakale. Pamenepo palibe kukambirana. Ngati mukufuna wakale, bwereranikoni. Ngati mukufuna wapanoyo ndiye zonse zakale muzisiye ndiye akukhulupirirani. 

Ndine DW ku Zomba, ndili ndi chibwenzi ndipo timakondana, koma pamene adachoka kupita ku holiday tidangolankhulana masiku ochepa, koma pano kuimba sakuyankha. Nditani?

DW,

Penapake timathamangira kuweruza pamene tilibe mfundo yogwirika. Kusayankha foni pena sizitanthauza kuti munthuyo wapeza wina. Dikirani adzabwerenso kapena adzayankhe foni ndipo mudzamve chimene chidamupangitsa kuti asamayankhe. Ngati sadzabweranso ndiye basi mutayeni.

Avatar
ANATCHEZERA
Previous Post

Bonang Matheba: South Africa Media Pesonality And Businesswoman

Next Post

‘Kudali ku FDH Bank’

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
fdh 1 | The Nation Online

‘Kudali ku FDH Bank’

Opinions and Columns

Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

April 18, 2021
Political Uncensored

Mighty mess!

April 18, 2021
My Thought

Chakwera’s indecisiveness will be his downfall

April 18, 2021
People’s Tribunal

Cut the crap, act on abuse forthwith

April 17, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Minister of Labour Ken Kandodo

    Ministry defends ‘borrowing’ of Covid-19 funds

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera bites

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chilima in public projects inspection

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • OPC frustrates roads projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malewezi’s career, political profile

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.