Monday, May 23, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Aphungu akwangula zokambirana zawo

by Steven Pembamoyo
09/04/2022
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mtsogoleri wa Nyumba ya Malamulo a Richard Chimwendo Banda adatseka mkumano wa aphungu Lachitatu ndi langizo kwa otsutsa boma kuti aonjezere mphamvu zawo kuti boma liziyenda bwino.

A Chimwendo amatseka mkumanowo pomwenso adakambirana za ndondomeko ya zachuma ya 2022 mpaka 2023 yomwe aphunguwo adavomereza kuti boma ligwiritse ntchito ndalama zokwana K2.84 triliyoni atakumana kwa sabata 9.

Nduna ya zachuma a Sosten Gwengwe adapereka ndondomeko ya zachuma

Iwo adati boma limayenda bwino ngati mbali yotsutsa ikuonetsa mphamvu poongolera momwe boma likuyendetsera zitukuko zake koma mmalo mwake, mbali yotsutsa boma ikutaya nthawi n’kumangolimbana.

“Tikufuna muzititsutsa osati muzingokangana. Mwangokhala zaka zitatu zokha kotsutsa koma mwagawikana kale nanga komwe mudzakwanitsile zaka 26 ngati anzanufe mbali yotsutsa idzakhalapo,” adatero a Chimwendo Banda.

Kadaulo pa ndale a Ernest Thindwa adayamikira a Chimwendo palangizo lawolo koma adati boma lisamadikile kutsutsidwa kuti lizipanga zooneka chifukwa lidapanga kale ndondomeko yamomwe lidzayendetsele dziko.

“A Chimwendo Banda akunena zoona, mbali yotsutsa imayenera kukhala ya mphamvu kuti boma lisamachite zopepera. Mutengere chitsanzo cha momwe malemu Bingu Wa Mutharika adayendetsera dziko zaka 5 zoyambirira chifukwa otsutsa nthawi imeneyo samasekerera.

“Komabe boma nalo lisamathawire koti silikutsutsidwa mokwanira chifukwa chitukuko sichidikira kutsutsidwa kokhakokha. Otsutsa amangothandizira kuti pomwe pakupotoka paongoke,” adatero a Thindwa.

Mkulu wa mbali yotsutsa boma a Kondwani Nankhumwa adayamikira aphungu podutsitsa bajeti koma adadzudzula zinthu zambiri zomwe sizikuyenda bwino mdziko muno.

“Amalawi akuzunzika chifukwa cha kukwera kwa mitengo ya zinthu. Mafuta ophikira lita imodzi pano ndi K4 000 pomwe malita 5 ndi K20 000. Buledi anali K500 pano ndi K1 000, sopo wa U-fresh adachoka pa K150 pano ndi K300 pomwe shuga adali K800 pano ndi K1 000,” adatero a Nankhumwa.

Iwo adapitiriza kudzudzula pulogalamu ya zipangizo zaulimi zotsika mtengo (AIP), katangale, kufooka kwa chitetezo, ufulu wa atolankhani, njala m’chaka chikubwerachi ndi kusayendetsa bwino chuma cha boma.

“Chaka ndi chaka timadutsitsa bajeti koma sitiunika bwinobwino kuti bajeti ya chaka chatha idayenda bwanji n’chifukwa chake zoipa zomwezi zimapeza malo,” adatero a Nankhumwa.

Nyumbayo idavomereza bajeti ya K2.84 triliyoni osasintha kalikonse koma mkulu wa bungwe la Human Rights Consultative Committee (HRCC) a Robert Mkwezalamba adati aphunguwo aziunika bajeti mwaukadaulo.

“Sitikudziwa kuti kapena bajetiyo idakonzedwa mwaukatswiri kapena aphunguwo adalibe luntha lozukuta bajeti. Mtsogolo muno tidzakonda kuti aphungu azilimbana nayo kwambiri bajeti osamangodutsitsa ayi,” adatero a Mkwezalamba.

Aphunguwo adavomereza mabilo 20 omwe akudikira kuti mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera asainire, adalandira malipoti okhudza ndende komanso lipoti la pachaka la nthambi yothana ndi katangale ndi lipoti lokhudza kayendetsedwe ka chuma.

Nduna zosiyanasiyana zidapereka malipoti a kumaunduna kwawo, makomiti osiyanasiyana adaperekanso malipoti awo, aphungu adali ndi mpata ofusa mafunso kwa nduna ndipo nyumbayo idavomereza mkulu wa majaji komanso membala wa nthambi yoyendetsa Nyumba ya Malamulo.

Previous Post

OVP should practice the austerity it preaches

Next Post

Reliving thirst and hunger for education

Related Posts

Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

May 22, 2022
Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
Next Post

Reliving thirst and hunger for education

Discussion about this post

Opinions and Columns

People’s Tribunal

What was that press briefing all about?

May 22, 2022
Big Man Wamkulu

Wife, in-law plotting my downfall

May 22, 2022
My Thought

Tonse Alliance died on arrival

May 22, 2022
Layman's Reflection

New IMF programme pivotal moment for Tonse Alliance

May 21, 2022

Trending Stories

  • Musician Martse in hospital after fire accident

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi overlooks players diet

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • How loans get wasted

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Gaba comes up with two options

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Onesimus leaves Major One Records

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.