Monday, May 16, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Mabishopu akunena zoona—akadaulo

by Steven Pembamoyo
11/03/2022
in Nkhani
4 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Akatswiri pa nkhani za ndale adandaula ndi kusasintha kwa zinthu m’dziko lino kwa zomwe zakhala zikuchitika kwa zaka zambiri.

Mwa zina, kusasinthaku kukuoneka pa nkhani za katangale, kusiyana kwambiri pakati pa olemera ndi osauka, kusankhana mitundu, kulowa pansi kwa maphunziro komanso kulowa pansi kwa ntchito zaumoyo.

Mafuta akwera mtengo kwambiri

Mmodzi mwa akatswiriwa, a Makhumbo Munthali adayankhula izi mabishopu a chikatolika atatulutsa chikalata chawo pokumbukira kuti padutsa zaka 30 chilembereni chikalata chotchedwa kuti ‘Kukhala moyo m’chikhulupiliro chathu’ chomwe chidadzudzulanso boma panthawiyo.

M’chikalatachi chomwe chidatuluka Lamulungu, atsogoleri a mpingowo adandaulanso kuti utsogoleri wa Boma la Tonse ukufooka komanso kuti ukumachedwa kumanga mfundo ngakhale pali malamulo owalola kuchita zinthu m’nthawi yake, makamaka pa nkhani yolimbana ndi katangale.

“Tikukhulupirira kuti mtsogoleri wa dziko amene adaachita kampeni potsamira pamfundo yolimbana ndi katangale ndiponso amene adalonjeza kuti athana ndi vutoli, sayenera kuikira kumbuyo nduna ndi omuthandizira ake omwe akuganiziridwa kuti adatenga nawo mbali pankhani yokhudza mchitidwewu, makamaka pamene pali umboni wokwanira,” kalatayo ikutero.

A Munthali adati ndi chachidziwikire kuti ngakhale pali mbali zina zomwe tachita bwino, tikubwererabe mmbuyo monga dziko.

“Utsogoleri wathu komanso kusowa kwa chidwi chosintha zinthu, kusalikonda dziko, kuikira kumbuyo anthu akuba chuma cha boma, kukonderana anthu a mtundu umozi ndi zina zikulepheretsa kukwaniritsa zikhumbokhumbo za chikalata cha kukhala moyo m’chikhulupiliro chathu.

“Kalata yatsopanoyi idayenera kukhala yosangalalira kuti takwanitsa kufikira zolinga za kalata ya kukhala moyo m’chikhulupiliro chathu ya m’chaka cha 1992 koma ndi zachisoni kutengera madandaulo ochokera kwa ma Bishopu kuti zinthuzi sizidatheke,” adatero a Munthali.

Iwo adapempha utsogoleri wa mgwirizano wa Tonse kuti uchitepo kanthu pa zomwe atsogoleri a mpingo akuchita nazo nkhawa zi.

“Si koyamba anthu kudandaula za izi, anthu adandaulapo za mavuto amenewa m’magulu osiyanasiyana. Zinthuzi zikukhudza madandaulo osiyanasiyana omwe Amalawi ali nawo. Koma zikuoneka ngati boma likutenga nthawi kuchitapo kanthu kuti lithane ndi mavutowa.

“Boma likathana ndi mavutowa mmalo modikira atsogoleri a mpingo kuwakumbutsa kuti asamaikire kumbuyo adindo ochita katangale kapena kusawathandiza amene akulimbana ndi mchitidwewu,” iwo adatero.

Mneneri wa chipani cha Malawi Congress Party (MCP) chomwe chikutsogolera mgwirizano wa Tonse mbusa Maurice Munthali adakana kuyankhapo pa nkhaniyi ponena kuti si koyenera kuti monga a chipani alowelere za kayendetsedwe ka boma koma mneneri wa boma ndi yemwe angayankhepo pa nkhaniyi.

Koma m’kuyankha kwawo, mneneri wa boma a Gospel Kazako adati ayankha kalatayo pambuyo akayiwerenga ndi kufotokoza zomwe boma lidakwanitsa kale kuchitako molingana ndi madandaulo omwe ali m’chikalatacho.

Iwo adatinso afotokoza zonse zomwe boma lili pafupi kuchita molingana ndi zomwe kalatayo yadandaulapo kuti Amalawi azikhala moyo wabwino.

“Kalatayo tayilandira ndi nsangala. Ife monga boma timatenga anzathu a mpingo wa Katolika ngati bwenzi lodalirika pankhani za chitukuko cha dziko lino, ndipo timalemekeza mawu ndi thandizo lawo,” adatero a Kazako.

Mfumu yaikulu Mwankhunikira ya ku Rumphi adavomereza kuti makamaka pankhani ya za chuma zinthu sizili bwino popeza anthu ambiri kuphatikizapo mafumuwo, malipiro awo akhala otsika kwa nthawi yaitali moti ndi mmene mitengo ya zinthu ikukwerera, sizikuyenda bwino.

“Kwa ife, utsogoleri wa Tonse uli bwinoko, koma anthu m’midzi akudandaula kwambiri ndi kukwera mtengo kwa zinthu monga mafuta a galimoto, mafuta ophikira, shuga, sopo, mchere ndi zinthu zina zofunikira pa moyo wa tsiku ndi tsiku choncho anthu osauka ku mudzi sakusangalala ndi moyo. Koma mwina popeza bomali ndi latsopano zinthu zikhoza kusintha mtsogolomu,” adatero amfumuwo.

Kuonjezera apo adandaulanso za kusowa kwa feteleza wotsika mtengo, kuti ngakhale anthu ali nazo ziphaso zogulira feterezayu, kufikira lero sadagulebe feterezayo ngakhale mvula yafika pachimake.

“Izi zikusonyeza kuti chaka chino kukhalanso njala popeza zokolola sizikhala zambiri kaamba koti anthu ambiri alephera kuthira feteleza m’nthawi yake,” adatero a Mwankhunikira.

Previous Post

Insurance faces credit, liquidity risks

Next Post

Boma lipereka katemera winanso wa polio

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post
A child gets the oral vaccine

Boma lipereka katemera winanso wa polio

Opinions and Columns

Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022
My Thought

Two years of nothing but development rallies

May 15, 2022

Trending Stories

  • Chakaka-Nyirenda: The DPP will look into it

    Embassy assets sold, money untraceable

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • PAC clears Macra director general, cautions board

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse cracks suspicions grow

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Two years of nothing but development rallies

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • My wife is a WhatsApp addict

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.