Monday, May 16, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

‘Ndinkafuna mnyamata wamtali, wakuda’

by Nation Online
30/01/2022
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 Ubwenzi wa James Mdala ndi Asiyatu James unayamba pa September 22 2020, mumzinda wa Lilongwe. Awiriwo anali atakumana miyezi iwiri mmbuyo mwake.

James amagwira ntchito ngati dotolo wamkulu wa za mano pachipatala cha cha Kamuzu Central pomwe Asiyatu amagwira ntchito ya utolankhani pa wailesi ya Radio Islam.

“Pa chiyambi mayiwa anali mnzawo wa mnzanga, ndiye dzina lawo pokhala Asiyatu James, ine langa James Mdala, tidali ngati dad ndi daughter wake mpakana patadutsa miyezi iwiri, ndidapezeka ndawafunsira ubwenzi ndipo anandivomera,” analongosola James.

James akuti kupatula maonekedwe abwino a Asiyatu, anakopeka ndi makhalidwe ake.

Asiyatu ndi James adayamba ngati macheza

“Ndife a chipembezo cha Chisilamu ndipo chimalimbikitsa khalidwe labwino. Ndiye nditaona khalidwe lawo pa chipembezo komanso pa umunthu sindinachedwenso ayi koma kuwafunsira ubwenzi,” James adatero.

Pomwe Asiyatu anati mtima wake unagunda atakumana ndi James pomwe adapita kukamuona mnzake.

“Nditamuona, mtima wanga udagunda chifukwa cha maonekedwe ake omwe adandisangalatsa chifukwa ndi mnyamata wakuda ndi wamtali monga ndinkalotera,” adalongosola Asiyatu.

Iye adati awiriwo adayamba kucheza pambuyo pogawana nambala za foni ndipo zokamba za James zidali za chilungamo.

“Kudekha kwake, kukhulupirika komanso kudzichepetsa kwake zidandipatsa chikoka chifukwa ndi zomwe mtima wanga wakhala ukusakasaka. Kotero sindidachedwenso ndi kumutaitsa nthawi James ayi koma kumuvomera ubwenzi,” anatero Asiyatu.

Atakhala pa ubwenzi kwa chaka chimodzi, James ndi Asiyatu adadalitsa ukwati wawo pa 9 October 2021 pa mzikiti wa Wafa m’boma la Zomba ndipo adakasupira kuholo ya sekondale ya Malindi ku Zomba konko.

Iwo akulangiza achinyamata onse omwe adapeza mnzawo woti amange naye banja ndipo akhutitsidwa naye, kuti asachedwe koma adalitse mabanja awo.

“Kwa atsikana anzanga, chomwe ndingawalangize ndiye kuyedzamira mwa Mulungu basi popeza Iye ndi amene amamuongolera munthu kunjira yabwino yopezera mamuna kapena mkazi,” anatero Asiyatu.

Pomwe James amachokera m’mudzi mwa Chongo, Mfumu Chikowi, m’boma la Zomba, Asiyatu amachokera m’mudzi mwa Chilipa, Mfumu Chilipa m’boma la Mangochi.

Pakadalipano iwo akukhalira ku Area 10, mumzinda wa Lilongwe.

Previous Post

Anatchereza

Next Post

Airtel Malawi spoils Flames

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post

Airtel Malawi spoils Flames

Opinions and Columns

Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022
My Thought

Two years of nothing but development rallies

May 15, 2022

Trending Stories

  • Chakaka-Nyirenda: The DPP will look into it

    Embassy assets sold, money untraceable

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • PAC clears Macra director general, cautions board

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse cracks suspicions grow

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Two years of nothing but development rallies

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • My wife is a WhatsApp addict

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.